< Miyambo 22 >

1 Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
A [good] name is rather to be chosen than great riches, [and] loving favour rather than silver and gold.
2 Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
The rich and the poor meet together: the LORD is the maker of them all.
3 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
A prudent man seeth the evil, and hideth himself: but the simple pass on, and suffer for it.
4 Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
The reward of humility [and] the fear of the LORD [is] riches, and honour, and life.
5 Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
Thorns [and] snares are in the way of the froward: he that keepeth his soul shall be far from them.
6 Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
Train up a child in the way he should go, and even when he is old he will not depart from it.
7 Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
The rich ruleth over the poor, and the borrower is servant to the lender.
8 Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
He that soweth iniquity shall reap calamity: and the rod of his wrath shall fail.
9 Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
He that hath a bountiful eye shall be blessed; for he giveth of his bread to the poor.
10 Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
Cast out the scorner, and contention shall go out; yea, strife and ignominy shall cease.
11 Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
He that loveth pureness of heart, [for] the grace of his lips the king shall be his friend.
12 Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
The eyes of the LORD preserve [him that hath] knowledge, but he overthroweth the words of the treacherous man.
13 Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
The sluggard saith, There is a lion without: I shall be murdered in the streets.
14 Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
The mouth of strange women is a deep pit: he that is abhorred of the LORD shall fall therein.
15 Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
Foolishness is bound up in the heart of a child; [but] the rod of correction shall drive it far from him.
16 Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
He that oppresseth the poor to increase his [gain, and] he that giveth to the rich, [cometh] only to want.
17 Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
Incline thine ear, and hear the words of the wise, and apply thine heart unto my knowledge.
18 Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
For it is a pleasant thing if thou keep them within thee, if they be established together upon thy lips.
19 Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
That thy trust may be in the LORD, I have made [them] known to thee this day, even to thee.
20 Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
Have not I written unto thee excellent things of counsels and knowledge;
21 malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
To make thee know the certainty of the words of truth, that thou mayest carry back words of truth to them that send thee?
22 Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
Rob not the poor, because he is poor, neither oppress the afflicted in the gate:
23 pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
For the LORD will plead their cause, and despoil of life those that despoil them.
24 Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
Make no friendship with a man that is given to anger; and with a wrathful man thou shalt not go:
25 kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
Lest thou learn his ways, and get a snare to thy soul.
26 Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
Be thou not one of them that strike hands, [or] of them that are sureties for debts:
27 ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
If thou hast not wherewith to pay, why should he take away thy bed from under thee?
28 Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
Remove not the ancient landmark, which thy fathers have set.
29 Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.
Seest thou a man diligent in his business? he shall stand before kings; he shall not stand before mean men.

< Miyambo 22 >