< Miyambo 22 >
1 Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
A good name is better than great riches: and good favour is above silver and gold.
2 Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
The rich and poor have met one another: the Lord is the maker of them both.
3 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
The prudent man saw the evil, and hid himself: the simple passed on, and suffered loss.
4 Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
The fruit of humility is the fear of the Lord, riches and glory and life.
5 Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
Arms and swords are in the way of the perverse: but he that keepeth his own soul departeth far from them.
6 Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
It is a proverb: A young man according to his way, even when he is old he will not depart from it.
7 Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
The rich ruleth over the poor: and the borrower is servant to him that lendeth.
8 Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
He that soweth iniquity shall reap evils, and with the rod of his anger he shall be consumed.
9 Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
He that is inclined to mercy shall be blessed: for of his bread he hath given to the poor. He that maketh presents shall purchase victory and honour: but he carrieth away the souls of the receivers.
10 Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
Cast out the scoffer, and contention shall go out with him, and quarrels and reproaches shall cease.
11 Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
He that loveth cleanness of heart, for the grace of his lips shall have the king for his friend.
12 Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
The eyes of the Lord preserve knowledge: and the words of the unjust are overthrown.
13 Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
The slothful man saith: There is a lion without, I shall be slain in the midst of the streets.
14 Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
The mouth of a strange woman is a deep pit: he whom the Lord is angry with, shall fall into it.
15 Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
Folly is bound up in the heart of a child, and the rod of correction shall drive it away.
16 Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
He that oppresseth the poor, to increase his own riches, shall himself give to one that is richer, and shall be in need.
17 Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
Incline thy ear, and hear the words of the wise: and apply thy heart to my doctrine:
18 Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
Which shall be beautiful for thee, if thou keep it in thy bowels, and it shall flow in thy lips:
19 Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
That thy trust may be in the Lord, wherefore I have also shewn it to thee this day.
20 Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
Behold I have described it to thee three manner of ways, in thoughts and knowledge:
21 malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
That I might shew thee the certainty, and the words of truth, to answer out of these to them that sent thee.
22 Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
Do no violence to the poor, because he is poor: and do not oppress the needy in the gate:
23 pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
Because the Lord will judge his cause, and will afflict them that have afflicted his soul.
24 Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
Be not a friend to an angry man, and do not walk with a furious man:
25 kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
Lest perhaps thou learn his ways, and take scandal to thy soul.
26 Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
Be not with them that fasten down their hands, and that offer themselves sureties for debts:
27 ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
For if thou have not wherewith to restore, what cause is there, that he should take the covering from thy bed?
28 Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
Pass not beyond the ancient bounds which thy fathers have set.
29 Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.
Hast thou seen a man swift in his work? he shall stand before kings, and shall not be before those that are obscure.