< Miyambo 22 >

1 Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
Et godt Navn er at foretrække for stor Rigdom; Gunst er bedre end Sølv og Guld.
2 Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
Rig og fattig mødtes; Herren har skabt dem alle.
3 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
Den kloge saa Ulykken og skjulte sig; men de uerfarne gik frem og maatte bøde.
4 Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
Løn for Sagtmodighed og Herrens Frygt er Rigdom og Ære og Liv.
5 Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
Torne og Snarer ere paa den forvendtes Vej; den, som vil bevare sin Sjæl, holde sig langt fra dem.
6 Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
Oplær den unge efter hans Vejs Beskaffenhed; endog naar han bliver gammel, skal han ikke vige derfra.
7 Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
Den rige hersker over de fattige; og den, som tager til Laans, bliver Træl for den Mand, som udlaaner.
8 Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
Hvo som saar Uret, skal høste Ulykke, og hans Grumheds Ris skal tages bort.
9 Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
Den, som har et godt Øje, skal velsignes; thi han gav den ringe af sit Brød.
10 Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
Uddriv Spotteren, saa gaar Trætten med, saa skal Kiv og Forsmædelse høre op.
11 Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
Den, som elsker Hjertets Renhed, hvis Læber ere yndige, hans Ven er Kongen.
12 Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
Herrens Øjne vaage over Kundskab, og han kuldkaster den troløses Ord.
13 Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
Den lade siger: Der er en Løve derude, jeg kunde blive revet ihjel midt paa Gaderne.
14 Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
Fremmede Kvinders Mund er en dyb Grav; den, Herren er vred paa, skal falde deri.
15 Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
Daarlighed er knyttet til den unges Hjerte; Tugtens Ris skal drive den langt fra ham.
16 Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
Hvo som fortrykker den ringe for at formere sit eget, og hvo som giver en rig, skal kun have Mangel.
17 Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
Bøj dit Øre, og hør de vises Ord, og vend dit Hjerte til min Kundskab!
18 Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
Thi det er yndigt, dersom du bevarer dem i dit Indre; de skulle alle være rede paa dine Læber.
19 Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
Paa det at din Tillid skal være til Herren, har jeg kundgjort det i Dag for dig, ja, for dig.
20 Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
Har jeg ikke skrevet dig ypperlige Ting med Raad og Undervisning
21 malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
for at kundgøre dig, hvad der er vist, Sandheds Ord, at du kan svare dem, som sendte dig, Ord, som ere Sandhed?
22 Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
Røv ikke fra den ringe, fordi han er ringe, og knus ikke den elendige for Retten.
23 pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
Thi Herren skal udføre deres Sag, og dem, som berøve dem, skal han berøve Livet.
24 Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
Hold ikke Selskab med en vredagtig Mand, og kom ikke til en hidsig Mand,
25 kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
at du ej skal lære hans Stier og faa en Snare for din Sjæl.
26 Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
Vær ikke iblandt dem, som give Haandslag, iblandt dem, som borge for Gæld.
27 ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
Dersom du intet har at betale med, hvorfor skulde man tage din Seng bort under dig?
28 Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
Flyt ikke det gamle Landemærke, som dine Fædre have sat.
29 Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.
Ser du en Mand, som er snar i sin Gerning, han skal stille sig frem for Konger, han skal ikke stille sig frem for uansete Mænd.

< Miyambo 22 >