< Miyambo 21 >

1 Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova; Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.
Во́дні пото́ки — царе́ве це серце в Господній руці: куди тільки захоче, його Він скеро́вує.
2 Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo, koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.
Всяка дорога люди́ни пряма́ в її о́чах, та керує серцями Госпо́дь.
3 Za chilungamo ndi zolondola ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.
Справедливість та правду чинити — для Господа це добірні́ше за жертву.
4 Maso odzikuza ndi mtima wonyada, zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.
Муж гордого ока та серця надутого — несправедливий, а світильник безбожних — це гріх.
5 Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake; koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.
Думки пильного лиш на достаток ведуть, а всякий квапли́вий — на збиток.
6 Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
Набува́ння майна язико́м неправдивим — це скоромину́ща марно́та шукаючих смерти.
7 Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga, pakuti iwo amakana kuchita zolungama.
Насильство безбожних пряму́є на них, бо пра́ва чинити не хо́чуть.
8 Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota, koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.
Дорога злочинця крута́, а чистий — прями́й його чин.
9 Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba, kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.
Ліпше жити в куті́ на даху́, ніж з сварливою жінкою в спі́льному домі.
10 Munthu woyipa amalakalaka zoyipa; sachitira chifundo mnansi wake wovutika.
Лихого жадає душа нечестивого, і в о́чах його ближній його не отримає милости.
11 Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru; koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.
Як карають глумли́вця мудріє безумний, а як мудрого вчать, — знання́ набуває.
12 Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova, ndipo Iye adzawononga woyipayo.
До дому свого пригляда́ється праведний, а безбожний дово́дить до зла.
13 Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira, nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.
Хто вухо своє затикає від зо́йку убогого, то й він буде кликати, та не отримає відповіді.
14 Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo, ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.
Таємний дару́нок пога́шує гнів, а нея́вний гости́нець — лють сильну.
15 Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala, koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.
Радість праведному — правосу́ддя чинити, а злочи́нцеві — страх.
16 Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.
Люди́на, що зблуджує від путі розуму, у зборі померлих спочине.
17 Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi, ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
Хто любить весе́лощі, той немаю́чий, хто любить вино та оливу, той не збагаті́є.
18 Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.
Безбожний — то викуп за праведного, а лукавий — за щирого.
19 Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.
Ліпше сидіти в пусти́нній країні, ніж з сварливою та сердитою жінкою.
20 Munthu wanzeru samwaza chuma chake, koma wopusa amachiwononga.
Скарб цінни́й та олива в мешка́нні премудрого, та нищить безумна люди́на його.
21 Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika, amapeza moyo ndi ulemerero.
Хто жене́ться за праведністю та за милістю, той знахо́дить життя, справедливість та славу.
22 Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.
До міста хоробрих уві́йде премудрий, і тверди́ню наді́ї його поруйнує.
23 Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake sapeza mavuto.
Хто стереже свої уста й свого язика́, той душу свою зберігає від лиха.
24 Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,” iye amachita zinthu modzitama kwambiri.
Надутий пихо́ю — насмішник ім'я́ йому, він робить усе із бундю́чним зухва́льством.
25 Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.
Пожада́ння лінивого вб'є його, бо руки його відмовляють робити, —
26 Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri, koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.
він кожного дня пожадли́во жадає, а справедливий дає та не жалує.
27 Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova, nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!
Жертва безбожних — оги́да, а надто тоді, як за ді́ло безчесне прино́ситься.
28 Mboni yonama idzawonongeka, koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.
Свідок брехливий загине, а люди́на, що слухає Боже, говори́тиме за́вжди.
29 Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima, koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.
Безбожна люди́на жорстока обличчям своїм, а невинний зміцня́є дорогу свою.
30 Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova.
Нема мудрости, ані розуму, ані ради насу́проти Господа.
31 Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo, koma ndi Yehova amene amapambanitsa.
Приготовлений кінь на день бо́ю, але́ перемога від Господа!

< Miyambo 21 >