< Miyambo 21 >
1 Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova; Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.
COMO los repartimientos de las aguas, así está el corazón del rey en la mano de Jehová: á todo lo que quiere lo inclina.
2 Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo, koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.
Todo camino del hombre es recto en su opinión: mas Jehová pesa los corazones.
3 Za chilungamo ndi zolondola ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.
Hacer justicia y juicio es á Jehová más agradable que sacrificio.
4 Maso odzikuza ndi mtima wonyada, zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.
Altivez de ojos, y orgullo de corazón, y el brillo de los impíos, son pecado.
5 Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake; koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.
Los pensamientos del solícito ciertamente [van] á abundancia; mas todo presuroso, indefectiblemente á pobreza.
6 Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
Allegar tesoros con lengua de mentira, es vanidad desatentada de aquellos que buscan la muerte.
7 Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga, pakuti iwo amakana kuchita zolungama.
La rapiña de los impíos los destruirá; por cuanto no quisieron hacer juicio.
8 Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota, koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.
El camino del hombre perverso es torcido y extraño: mas la obra del limpio es recta.
9 Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba, kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.
Mejor es vivir en un rincón de zaquizamí, que con la mujer rencillosa en espaciosa casa.
10 Munthu woyipa amalakalaka zoyipa; sachitira chifundo mnansi wake wovutika.
El alma del impío desea mal: su prójimo no le parece bien.
11 Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru; koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.
Cuando el escarnecedor es castigado, el simple se hace sabio; y cuando se amonestare al sabio, aprenderá ciencia.
12 Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova, ndipo Iye adzawononga woyipayo.
Considera el justo la casa del impío: [cómo] los impíos son trastornados por el mal.
13 Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira, nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.
El que cierra su oído al clamor del pobre, también él clamará, y no será oído.
14 Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo, ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.
El presente en secreto amansa el furor, y el don en el seno, la fuerte ira.
15 Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala, koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.
Alegría es al justo hacer juicio; mas quebrantamiento á los que hacen iniquidad.
16 Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.
El hombre que se extravía del camino de la sabiduría, vendrá á parar en la compañía de los muertos.
17 Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi, ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
Hombre necesitado será el que ama el deleite: y el que ama el vino y ungüentos no enriquecerá.
18 Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.
El rescate del justo es el impío, y por los rectos el prevaricador.
19 Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.
Mejor es morar en tierra del desierto, que con la mujer rencillosa é iracunda.
20 Munthu wanzeru samwaza chuma chake, koma wopusa amachiwononga.
Tesoro codiciable y pingüe hay en la casa del sabio; mas el hombre insensato lo disipará.
21 Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika, amapeza moyo ndi ulemerero.
El que sigue la justicia y la misericordia, hallará la vida, la justicia, y la honra.
22 Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.
La ciudad de los fuertes tomó el sabio, y derribó la fuerza en que ella confiaba.
23 Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake sapeza mavuto.
El que guarda su boca y su lengua, su alma guarda de angustias.
24 Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,” iye amachita zinthu modzitama kwambiri.
Soberbio y presuntuoso escarnecedor es el nombre del que obra con orgullosa saña.
25 Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.
El deseo del perezoso le mata, porque sus manos no quieren trabajar.
26 Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri, koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.
Hay quien todo el día codicia: mas el justo da, y no desperdicia.
27 Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova, nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!
El sacrificio de los impíos es abominación: ¡cuánto más ofreciéndolo con maldad!
28 Mboni yonama idzawonongeka, koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.
El testigo mentiroso perecerá: mas el hombre que oye, permanecerá en su dicho.
29 Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima, koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.
El hombre impío afirma su rostro: mas el recto ordena sus caminos.
30 Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova.
No hay sabiduría, ni inteligencia, ni consejo, contra Jehová.
31 Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo, koma ndi Yehova amene amapambanitsa.
El caballo se apareja para el día de la batalla: mas de Jehová es el salvar.