< Miyambo 21 >
1 Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova; Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.
HE mau auwai ka naau o ke alii, iloko o ka lima o Iehova, Nana e hookahe ae e like me kona makemake.
2 Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo, koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.
O na aoao a pau o ke kanaka, ua pololei ia i kona maka iho, Hoao ae la o Iehova i na naau.
3 Za chilungamo ndi zolondola ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.
O ka hana ana i ka pono a me ka pololei, Ua makemakeia e Iehova mamua o ka mohai.
4 Maso odzikuza ndi mtima wonyada, zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.
O ka maka haaheo, o ka naau hookiekie, O ka pomaikai ana hoi o ka poe hewa he pono ole no ia.
5 Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake; koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.
O ka manao o ka mea hana mau, pili no ia i ka lako; O ko ka mea wikiwiki wale, pili no ia i ka nele.
6 Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
O ka imi ana i ka waiwai ma ke elelo wahahee, He opala i hoopuehuia e ka poe e imi ana i ka make.
7 Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga, pakuti iwo amakana kuchita zolungama.
O ke kaili wale o ka poe hewa, e kaili aku ia ia lakou; No ka mea, hoole lakou, aole e hana ma ka hoopono.
8 Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota, koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.
He kekee ka aoao o ke kanaka, a he ano e hoi; O ka mea maemae hoi, ua pololei kana hana.
9 Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba, kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.
E aho ka noho ma ke kihi maluna o ka hale, Aole hoi me ka wahine hakaka ma ka hale kanaka.
10 Munthu woyipa amalakalaka zoyipa; sachitira chifundo mnansi wake wovutika.
O ka uhane o ka mea hewa, makemake no ia i ka hewa; Aole ona lokomaikai mai i kona hoanoho.
11 Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru; koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.
Ma ka hoopaiia mai o ka mea hoowahawaha, e hoonaauaoia'i ka mea ike ole; I ke ao ana aku i ka mea akamai, e loaa no ia ia ka ike.
12 Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova, ndipo Iye adzawononga woyipayo.
Noonoo nui ka mea pono i ka hale o ka mea hewa; Ua hookahuliia ka poe hewa no ka hana hewa ana.
13 Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira, nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.
O ka mea i papani i kona pepeiao i ka uwe ana o ka mea nele, E hea aku no oia, aohe mea e hoolohe mai.
14 Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo, ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.
O ka makana malu, pale ae no ia i ka huhu; Pela hoi ka makana poli i ka inaina ikaika.
15 Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala, koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.
He olioli i ka mea pono ke hana ma ka pololei; He make no ko ka poe hana hewa.
16 Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.
O ke kanaka hele hewa mai ka aoao ae o ka naauao, E noho no oia ma ke anaina o ka poe malu make.
17 Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi, ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
O ka mea makemake i ka lealea, e ilihune auanei ia, O ka mea makemake i ka waina a me ka aila, aole ia e waiwai.
18 Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.
Pani ka mea hewa i ka hakahaka no ka mea pono; Pela ka mea lawe hala no ka mea pololei.
19 Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.
E aho ka noho noho ana ma ka waoakua. Aole me ka wahine huhu a me ka hakaka.
20 Munthu wanzeru samwaza chuma chake, koma wopusa amachiwononga.
Aia ka waiwai i makemakeia a me ka aila ma ka hale o ka mea naauao; A o ke kanaka lapuwale, moni iho la oia ia mea.
21 Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika, amapeza moyo ndi ulemerero.
O ka mea hahai mahope o ka pono, a me ka lokomaikai, E loaa ia ia ke ola a me ka pono a me ka nani.
22 Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.
Pii ae ka mea naauao maluna o ke kulanakauhale o ka poe ikaika, Hoohiolo oia i ka ikaika a lakou i paulele ai.
23 Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake sapeza mavuto.
O ka mea malama i kona waha a me kona alelo, Oia ka i hoopakele i kona uhane i ka popilikia.
24 Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,” iye amachita zinthu modzitama kwambiri.
O ka haaheo, o ka hookano, o ka hoowahawaha, Oia ka inoa o ka mea hana ma ka huhu ikaika.
25 Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.
O ka makemake o ka mea palaualelo oia kona mea e make ai; No ka mea, hoole kona mau lima i ka hana.
26 Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri, koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.
Kuko wale aku no ia a po ka la; Haawi aku hoi ka mea pono me ka aua ole.
27 Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova, nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!
O ka mohai o ka poe hewa, he hoopailua ia; Ua oi aku hoi ka hewa, ke lawe oia ia mea me ka manao ino.
28 Mboni yonama idzawonongeka, koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.
O ka mea hoike wahahee, e make no ia; O ke kanaka hoolohe, oia ke olelo mau.
29 Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima, koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.
Hoopaakiki ke kanaka hewa i kona maka; O ka mea pololei hoi, hoopololei oia i kona aoao.
30 Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova.
Aohe akamai, aohe noonoo; Aole hoi oleloao e hiki ai ke ku e aku ia Iehova.
31 Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo, koma ndi Yehova amene amapambanitsa.
Ua hoomakaukauia ka lio no ka la e kaua ai; Aka, ia Iehova no ka hoopakele ana.