< Miyambo 21 >

1 Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova; Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.
Comme sont les courants des eaux, ainsi est le cœur du roi dans la main du Seigneur: de quelque côté qu’il veut, il le fera tourner.
2 Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo, koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.
Toute voie de l’homme lui paraît droite; mais le Seigneur pèse les cœurs.
3 Za chilungamo ndi zolondola ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.
Faire miséricorde et justice plaît plus au Seigneur que des victimes.
4 Maso odzikuza ndi mtima wonyada, zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.
L’exaltation des yeux vient de la dilatation du cœur: la lampe des impies est péché.
5 Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake; koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.
Les pensées d’un homme fort amènent toujours l’abondance; mais tout paresseux est toujours dans la détresse.
6 Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
Celui qui amasse des trésors avec une langue de mensonge est vain et sans cœur, et il s’engagera dans les lacs de la mort.
7 Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga, pakuti iwo amakana kuchita zolungama.
Les rapines des impies les entraîneront à leur ruine, parce qu’ils n’ont pas voulu faire justice.
8 Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota, koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.
La voie perverse d’un homme est une voie étrangère; mais celui qui est pur, son œuvre est droite.
9 Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba, kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.
Mieux vaut demeurer sur l’angle d’un toit qu’avec une femme querelleuse et dans une maison commune.
10 Munthu woyipa amalakalaka zoyipa; sachitira chifundo mnansi wake wovutika.
L’âme de l’impie désire le mal; il n’aura pas pitié de son prochain.
11 Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru; koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.
L’homme contagieux étant puni, le simple sera plus sage; et s’il s’attache à un sage, il acquerra de la science.
12 Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova, ndipo Iye adzawononga woyipayo.
Le juste réfléchit à la maison de l’impie, pour retirer les impies du mal.
13 Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira, nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.
Celui qui ferme son oreille au cri du pauvre criera lui-même et ne sera pas exaucé.
14 Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo, ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.
Un présent secret éteint les colères; et un don glissé dans le sein, l’indignation la plus grande.
15 Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala, koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.
C’est une joie pour le juste que de faire justice; mais c’est l’effroi de ceux qui opèrent l’iniquité.
16 Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.
L’homme qui s’égare de la voie de la doctrine demeurera dans l’assemblée des géants.
17 Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi, ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
Celui qui aime les festins sera dans la détresse: celui qui aime le vin et la bonne chère ne s’enrichira pas.
18 Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.
Pour le juste est livré l’impie, et pour les hommes droits l’homme inique.
19 Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.
Mieux vaut habiter dans une terre déserte qu’avec une femme querelleuse et colère.
20 Munthu wanzeru samwaza chuma chake, koma wopusa amachiwononga.
Il y a un trésor précieux et de l’huile dans la demeure du juste; mais l’homme imprudent les dissipera.
21 Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika, amapeza moyo ndi ulemerero.
Celui qui recherche la justice et la miséricorde trouvera la vie, la justice et la gloire.
22 Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.
Le sage a escaladé la cité des forts, et a détruit la force où elle mettait sa confiance.
23 Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake sapeza mavuto.
Celui qui garde sa bouche et sa langue garde son âme des angoisses.
24 Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,” iye amachita zinthu modzitama kwambiri.
L’homme superbe et arrogant est appelé ignorant, parce que dans la colère il agit avec orgueil.
25 Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.
Les désirs tuent le paresseux; car ses mains n’ont voulu rien faire.
26 Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri, koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.
Tout le jour il souhaite et il désire; mais le juste donnera et il ne cessera de donner.
27 Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova, nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!
Les hosties des impies sont abominables, parce qu’elles sont offertes comme fruit de leur crime.
28 Mboni yonama idzawonongeka, koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.
Le témoin menteur périra; l’homme obéissant parlera victoire.
29 Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima, koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.
L’homme impie affermit effrontément son visage; mais celui qui est droit corrige sa voie.
30 Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova.
Il n’y a pas de sagesse, il n’y a pas de prudence, il n’y a pas de conseil contre le Seigneur.
31 Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo, koma ndi Yehova amene amapambanitsa.
Le cheval est préparé pour le jour du combat; mais c’est le Seigneur qui donne la victoire.

< Miyambo 21 >