< Miyambo 21 >

1 Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova; Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.
The king’s heart is in the hand of the LORD as the watercourses: he turneth it whithersoever he will.
2 Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo, koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.
Every way of a man is right in his own eyes: but the LORD weigheth the hearts.
3 Za chilungamo ndi zolondola ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.
To do justice and judgment is more acceptable to the LORD than sacrifice.
4 Maso odzikuza ndi mtima wonyada, zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.
An high look, and a proud heart, [even] the lamp of the wicked, is sin.
5 Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake; koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.
The thoughts of the diligent [tend] only to plenteousness: but every one that is hasty [hasteth] only to want.
6 Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
The getting of treasures by a lying tongue is a vapour driven to and fro; they [that seek them] seek death.
7 Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga, pakuti iwo amakana kuchita zolungama.
The violence of the wicked shall sweep them away; because they refuse to do judgment.
8 Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota, koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.
The way of him that is laden with guilt is exceeding crooked: but as for the pure, his work is right.
9 Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba, kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.
It is better to dwell in the corner of the housetop, than with a contentious woman in a wide house.
10 Munthu woyipa amalakalaka zoyipa; sachitira chifundo mnansi wake wovutika.
The soul of the wicked desireth evil: his neighbour findeth no favour in his eyes.
11 Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru; koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.
When the scorner is punished, the simple is made wise: and when the wise is instructed, he receiveth knowledge.
12 Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova, ndipo Iye adzawononga woyipayo.
The righteous man considereth the house of the wicked; [how] the wicked are overthrown to [their] ruin.
13 Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira, nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.
Whoso stoppeth his ears at the cry of the poor, he also shall cry, but shall not be heard.
14 Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo, ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.
A gift in secret pacifieth anger, and a present in the bosom strong wrath.
15 Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala, koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.
It is joy to the righteous to do judgment; but it is a destruction to the workers of iniquity.
16 Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.
The man that wandereth out of the way of understanding shall rest in the congregation of the dead.
17 Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi, ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
He that loveth pleasure shall be a poor man: he that loveth wine and oil shall not be rich.
18 Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.
The wicked is a ransom for the righteous; and the treacherous [cometh] in the stead of the upright.
19 Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.
It is better to dwell in a desert land, than with a contentious and fretful woman.
20 Munthu wanzeru samwaza chuma chake, koma wopusa amachiwononga.
There is precious treasure and oil in the dwelling of the wise; but a foolish man swalloweth it up.
21 Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika, amapeza moyo ndi ulemerero.
He that followeth after righteousness and mercy findeth life, righteousness, and honour.
22 Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.
A wise man scaleth the city of the mighty, and bringeth down the strength of the confidence thereof.
23 Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake sapeza mavuto.
Whoso keepeth his mouth and his tongue keepeth his soul from troubles.
24 Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,” iye amachita zinthu modzitama kwambiri.
The proud and haughty man, scorner is his name, he worketh in the arrogance of pride.
25 Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.
The desire of the slothful killeth him; for his hands refuse to labour.
26 Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri, koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.
There is that coveteth greedily all the day long: but the righteous giveth and withholdeth not.
27 Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova, nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!
The sacrifice of the wicked is an abomination: how much more, when he bringeth it with a wicked mind!
28 Mboni yonama idzawonongeka, koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.
A false witness shall perish: but the man that heareth shall speak unchallenged.
29 Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima, koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.
A wicked man hardeneth his face: but as for the upright, he ordereth his ways.
30 Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova.
There is no wisdom nor understanding nor counsel against the LORD.
31 Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo, koma ndi Yehova amene amapambanitsa.
The horse is prepared against the day of battle: but victory is of the LORD,

< Miyambo 21 >