< Miyambo 21 >

1 Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova; Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.
As a rush of water, so is the king's heart in God's hand: he turns it wherever he may desire to point out.
2 Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo, koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.
Every man seems to himself righteous; but the Lord directs the hearts.
3 Za chilungamo ndi zolondola ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.
To do justly and to speak truth, are more pleasing to God than the blood of sacrifices.
4 Maso odzikuza ndi mtima wonyada, zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.
A high-minded man is stout-hearted in [his] pride; and the lamp of the wicked is sin.
5 Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake; koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.
6 Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
He that gathers treasures with a lying tongue pursues vanity [on] to the snares of death.
7 Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga, pakuti iwo amakana kuchita zolungama.
Destruction shall lodge with the ungodly; for they refuse to do justly.
8 Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota, koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.
To the froward God sends froward ways; for his works are pure and right.
9 Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba, kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.
[It is] better to dwell in a corner on the house-top, than in plastered [rooms] with unrighteousness, and in an open house.
10 Munthu woyipa amalakalaka zoyipa; sachitira chifundo mnansi wake wovutika.
The soul of the ungodly shall not be pitied by any man.
11 Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru; koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.
When an intemperate man is punished the simple becomes wiser: and a wise man understanding will receive knowledge.
12 Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova, ndipo Iye adzawononga woyipayo.
A righteous man understands the hearts of the ungodly: and despises the ungodly for their wickedness.
13 Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira, nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.
He that stops his ears from hearing the poor, himself also shall cry, and there shall be none to hear [him].
14 Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo, ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.
A secret gift calms anger: but he that forbears to give stirs up strong wrath.
15 Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala, koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.
[It is] the joy of the righteous to do judgment: but a holy [man] is abominable with evil-doers.
16 Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.
A man that wanders out of the way of righteousness, shall rest in the congregation of giants.
17 Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi, ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
A poor man loves mirth, loving wine and oil in abundance;
18 Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.
and a transgressor is the abomination of a righteous man.
19 Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.
[It is] better to dwell in a wilderness than with a quarrelsome and talkative and passionate woman.
20 Munthu wanzeru samwaza chuma chake, koma wopusa amachiwononga.
A desirable treasure will rest on the mouth of the wise; but foolish men will swallow it up.
21 Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika, amapeza moyo ndi ulemerero.
The way of righteousness and mercy will find life and glory.
22 Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.
A wise man assaults strong cities, and demolishes the fortress in which the ungodly trusted.
23 Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake sapeza mavuto.
He that keeps his mouth and his tongue keeps his soul from trouble.
24 Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,” iye amachita zinthu modzitama kwambiri.
A bold and self-willed and insolent [man] is called a pest: and he that remembers injuries is a transgressor.
25 Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.
Desires kill the sluggard; for his hands do not choose to do anything.
26 Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri, koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.
An ungodly man entertains evil desires all the day: but the righteous is unsparingly merciful and compassionate.
27 Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova, nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!
The sacrifices of the ungodly are abomination to the Lord, for they offer them wickedly.
28 Mboni yonama idzawonongeka, koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.
A false witness shall perish; but an obedient man will speak cautiously.
29 Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima, koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.
An ungodly man impudently withstands with his face; but the upright man himself understands his ways.
30 Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova.
There is no wisdom, there is no courage, there is no counsel against the ungodly.
31 Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo, koma ndi Yehova amene amapambanitsa.
A horse is prepared for the day of battle; but help is of the Lord.

< Miyambo 21 >