< Miyambo 21 >

1 Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova; Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.
The king's heart is in the hand of the LORD, as the rivers of water: he turns it anywhere he will.
2 Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo, koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.
Every way of a man is right in his own eyes: but the LORD ponders the hearts.
3 Za chilungamo ndi zolondola ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.
To do justice and judgment is more acceptable to the LORD than sacrifice.
4 Maso odzikuza ndi mtima wonyada, zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.
An high look, and a proud heart, and the plowing of the wicked, is sin.
5 Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake; koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.
The thoughts of the diligent tend only to plenteousness; but of every one that is hasty only to lack.
6 Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
The getting of treasures by a lying tongue is a vanity tossed back and forth of them that seek death.
7 Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga, pakuti iwo amakana kuchita zolungama.
The robbery of the wicked shall destroy them; because they refuse to do judgment.
8 Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota, koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.
The way of man is perverse and strange: but as for the pure, his work is right.
9 Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba, kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.
It is better to dwell in a corner of the housetop, than with a brawling woman in a wide house.
10 Munthu woyipa amalakalaka zoyipa; sachitira chifundo mnansi wake wovutika.
The soul of the wicked desires evil: his neighbour finds no favour in his eyes.
11 Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru; koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.
When the scorner is punished, the simple is made wise: and when the wise is instructed, he receives knowledge.
12 Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova, ndipo Iye adzawononga woyipayo.
The righteous man wisely considers the house of the wicked: but God overthrows the wicked for their wickedness.
13 Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira, nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.
Whoso stops his ears at the cry of the poor, he also shall cry himself, but shall not be heard.
14 Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo, ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.
A gift in secret pacifies anger: and a reward in the bosom strong wrath.
15 Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala, koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.
It is joy to the just to do judgment: but destruction shall be to the workers of iniquity.
16 Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.
The man that wanders out of the way of understanding shall remain in the congregation of the dead.
17 Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi, ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
He that loves pleasure shall be a poor man: he that loves wine and oil shall not be rich.
18 Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.
The wicked shall be a ransom for the righteous, and the transgressor for the upright.
19 Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.
It is better to dwell in the wilderness, than with a contentious and an angry woman.
20 Munthu wanzeru samwaza chuma chake, koma wopusa amachiwononga.
There is treasure to be desired and oil in the dwelling of the wise; but a foolish man spends it up.
21 Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika, amapeza moyo ndi ulemerero.
He that follows after righteousness and mercy finds life, righteousness, and honour.
22 Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.
A wise man scales the city of the mighty, and casts down the strength of the confidence thereof.
23 Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake sapeza mavuto.
Whoso keeps his mouth and his tongue keeps his soul from troubles.
24 Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,” iye amachita zinthu modzitama kwambiri.
Proud and haughty scorner is his name, who deals in proud wrath.
25 Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.
The desire of the slothful kills him; for his hands refuse to labour.
26 Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri, koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.
He covers greedily all the day long: but the righteous gives and spares not.
27 Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova, nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!
The sacrifice of the wicked is abomination: how much more, when he brings it with a wicked mind?
28 Mboni yonama idzawonongeka, koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.
A false witness shall perish: but the man that hears speaks constantly.
29 Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima, koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.
A wicked man hardens his face: but as for the upright, he directs his way.
30 Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova.
There is no wisdom nor understanding nor counsel against the LORD.
31 Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo, koma ndi Yehova amene amapambanitsa.
The horse is prepared against the day of battle: but safety is of the LORD.

< Miyambo 21 >