< Miyambo 21 >

1 Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova; Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.
En Konges hjerte er Bække i HERRENs hånd, han leder det hen, hvor han vil.
2 Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo, koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.
En Mand holder al sin Færd for ret, men HERREN vejer Hjerter.
3 Za chilungamo ndi zolondola ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.
At øve Ret og Skel er mere værd for HERREN end Offer.
4 Maso odzikuza ndi mtima wonyada, zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.
Hovmodige Øjne, et opblæst Hjerte, selv gudløses Nyjord er Synd.
5 Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake; koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.
Kun Overflod bringer den flittiges Råd, hver, som har Hastværk, får kun Tab.
6 Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
At skabe sig Rigdom ved Løgnetunge er Jag efter Vind i Dødens Snarer.
7 Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga, pakuti iwo amakana kuchita zolungama.
Gudløses Voldsfærd bortriver dem selv, thi de vægrer sig ved at øve Ret.
8 Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota, koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.
Skyldtynget Mand går Krogveje, den renes Gerning er ligetil.
9 Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba, kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.
Hellere bo i en Krog på Taget end fælles Hus med frættekær Kvinde.
10 Munthu woyipa amalakalaka zoyipa; sachitira chifundo mnansi wake wovutika.
Den gudløses Sjæl har Lyst til ondt, hans Øjne ynker ikke hans Næste.
11 Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru; koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.
Må Spotter bøde, bliver tankeløs klog, har Vismand Fremgang, da vinder han kundskab.
12 Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova, ndipo Iye adzawononga woyipayo.
Den Retfærdige har Øje med den gudløses Hus, han styrter gudløse Folk i Ulykke.
13 Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira, nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.
Hvo Øret lukker for Småmands Skrig, skal råbe selv og ikke få Svar.
14 Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo, ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.
Lønlig Gave mildner Vrede, Stikpenge i Brystfolden voldsom Harme.
15 Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala, koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.
Rettens Gænge er den retfærdiges Glæde, men Udådsmændenes Rædsel.
16 Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.
Den, der farer vild fra Kløgtens Vej, skal havne i Skyggers Forsamling.
17 Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi, ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
Lyst til Morskab fører i Trang, Lyst til Olie og Vin gør ej rig.
18 Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.
Den gudløse bliver Løsepenge for den retfærdige, den troløse kommer i retsindiges Sted.
19 Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.
Hellere bo i et Ørkenland end hos en trættekær, arrig Kvinde.
20 Munthu wanzeru samwaza chuma chake, koma wopusa amachiwononga.
I den vises Bolig er kostelig Skat og Olie, en Tåbe af et Menneske øder det.
21 Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika, amapeza moyo ndi ulemerero.
Den, der higer efter Retfærd og Godhed vinder sig Liv og Ære.
22 Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.
Vismand stormer Heltes By og styrter Værnet, den stolede på.
23 Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake sapeza mavuto.
Den, der vogter sin Mund og sin Tunge, vogter sit Liv for Trængsler. -
24 Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,” iye amachita zinthu modzitama kwambiri.
Den opblæste stolte kaldes en Spotter, han handler frækt i Hovmod.
25 Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.
Den lades Attrå bliver hans Død, thi hans Hænder vil intet bestille.
26 Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri, koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.
Ugerningsmand er stadig i Trang, den retfærdige giver uden at spare.
27 Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova, nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!
Vederstyggeligt er de gudløses Offer, især når det ofres for Skændselsdåd.
28 Mboni yonama idzawonongeka, koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.
Løgnagtigt Vidne går under, Mand, som vil høre, kan tale fremdeles.
29 Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima, koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.
Den gudløse optræder frækt, den retsindige overtænker sin Vej.
30 Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova.
Visdom er intet, Indsigt er intet, Råd er intet over for HERREN.
31 Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo, koma ndi Yehova amene amapambanitsa.
Hest holdes rede til Stridens Dag, men Sejren er HERRENs Sag.

< Miyambo 21 >