< Miyambo 21 >

1 Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova; Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.
Kongens Hjerte i Herrens Haand er Vandbække; til alt det, han vil, bøjer han det.
2 Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo, koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.
Alle en Mands Veje ere rette for hans egne Øjne; men Herren vejer Hjerter.
3 Za chilungamo ndi zolondola ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.
At øve Retfærdighed og Ret er Herren kærere end Offer.
4 Maso odzikuza ndi mtima wonyada, zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.
Øjnenes Hovmod og Hjertets Stolthed, de ugudeliges Lampe, er Synd.
5 Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake; koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.
Den flittiges Tanker bringe kun Overflod, men den ilfærdiges bringe det kun til Mangel.
6 Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
At arbejde paa at samle Liggendefæ ved en falsk Tunge er Dunst, som bortvejres hos dem, som søge Døden.
7 Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga, pakuti iwo amakana kuchita zolungama.
De ugudeliges Ødelæggelse river dem bort; thi de have vægret sig ved at gøre Ret.
8 Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota, koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.
En skyldbetynget Mand gaar Krogveje; men den renes Gerning er ligefrem.
9 Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba, kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.
Det er bedre at bo i et Hjørne paa Taget end hos en trættekær Kvinde og i Hus sammen.
10 Munthu woyipa amalakalaka zoyipa; sachitira chifundo mnansi wake wovutika.
Den ugudeliges Sjæl har Lyst til det onde; hans Ven finder ikke Naade for hans Øjne.
11 Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru; koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.
Naar man lægger Straf paa en Spotter, bliver den uerfarne viis, og naar man belærer den vise, skal han modtage Kundskab.
12 Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova, ndipo Iye adzawononga woyipayo.
Den retfærdige agter paa den ugudeliges Hus, naar det styrter de ugudelige i Ulykke.
13 Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira, nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.
Hvo som stopper sit Øre for den ringes Raab, han, ja, han skal raabe og ikke bønhøres.
14 Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo, ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.
En Gave i Løndom stiller Vrede, og en Skænk i Smug stiller heftig Fortørnelse.
15 Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala, koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.
Det bliver den retfærdige en Glæde at have gjort Ret; men der er Fordærvelse for dem, som gøre Uret.
16 Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.
Et Menneske, som farer vild fra Klogskabs Vej, skal hvile i Dødningers Forsamling.
17 Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi, ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
Den, som elsker Glæde, skal have Mangel; den, som elsker Vin og Olie, skal ikke blive rig.
18 Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.
Den ugudelige bliver Løsepenge for den retfærdige og den troløse for de oprigtige.
19 Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.
Det er bedre at bo i et øde Land end hos en trættekær og arrig Kvinde.
20 Munthu wanzeru samwaza chuma chake, koma wopusa amachiwononga.
I den vises Bolig er der kosteligt Liggendefæ og Olie; men et daarligt Menneske opsluger det.
21 Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika, amapeza moyo ndi ulemerero.
Hvo der søger efter Retfærdighed og Miskundhed, skal finde Liv, Retfærdighed og Ære.
22 Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.
Den vise stormede de vældiges Stad og nedstyrtede dens sikre Værn.
23 Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake sapeza mavuto.
Hvo der bevarer sin Mund og sin Tunge, bevarer sin Sjæl fra Trængsler.
24 Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,” iye amachita zinthu modzitama kwambiri.
Den pralende stolte, hans Navn er Spotter; han handler i Stoltheds Overmod.
25 Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.
Den lades Begæring dræber ham; thi hans Hænder have vægret sig ved at gøre noget.
26 Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri, koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.
Han begærer og begærer den hele Dag; men den retfærdige giver og holder ikke tilbage.
27 Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova, nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!
De ugudeliges Offer er en Vederstyggelighed, meget mere naar de bringe det med et skændigt Forsæt.
28 Mboni yonama idzawonongeka, koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.
Et løgnagtigt Vidne skal omkomme; men en Mand, som hører efter, vil altid kunne tale igen.
29 Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima, koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.
En ugudelig Mand forhærder sit Ansigt; men den oprigtige han befæster sin Vej.
30 Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova.
Der gælder ikke Visdom, ej heller Forstand, ej heller Raad over for Herren.
31 Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo, koma ndi Yehova amene amapambanitsa.
Hesten beredes til Krigens Dag, men Frelsen hører Herren til.

< Miyambo 21 >