< Miyambo 20 >

1 Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
EL vino es escarnecedor, la cerveza alborotadora; y cualquiera que por ello errare, no será sabio.
2 Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
Como bramido de cachorro de león es el terror del rey: el que lo hace enfurecerse, peca [contra] su alma.
3 Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
Honra es del hombre dejarse de contienda: mas todo insensato se envolverá [en ella].
4 Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
El perezoso no ara á causa del invierno; pedirá pues en la siega, y no [hallará].
5 Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
[Como] aguas profundas es el consejo en el corazón del hombre: mas el hombre entendido lo alcanzará.
6 Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
Muchos hombres publican cada uno su liberalidad: mas hombre de verdad, ¿quién lo hallará?
7 Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
El justo que camina en su integridad, bienaventurados serán sus hijos después de él.
8 Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
El rey que se sienta en el trono de juicio, con su mirar disipa todo mal.
9 Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
¿Quién podrá decir: Yo he limpiado mi corazón, limpio estoy de mi pecado?
10 Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
Doble pesa y doble medida, abominación son á Jehová ambas cosas.
11 Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
Aun el muchacho es conocido por sus hechos, si su obra fuere limpia y recta.
12 Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
El oído que oye, y el ojo que ve, ambas cosas ha igualmente hecho Jehová.
13 Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
No ames el sueño, porque no te empobrezcas; abre tus ojos, [y] te hartarás de pan.
14 Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
El que compra dice: malo es, malo es: mas en apartándose, se alaba.
15 Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
Hay oro y multitud de piedras preciosas: mas los labios sabios son vaso precioso.
16 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
Quítale su ropa al que salió por fiador del extraño; y tómale prenda [al que fía] la extraña.
17 Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
Sabroso es al hombre el pan de mentira; mas después su boca será llena de cascajo.
18 Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
Los pensamientos con el consejo se ordenan: y con industria se hace la guerra.
19 Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
El que descubre el secreto, en chismes anda: no te entrometas, pues, con el que lisonjea con sus labios.
20 Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
El que maldice á su padre ó á su madre, su lámpara será apagada en oscuridad tenebrosa.
21 Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
La herencia adquirida de priesa al principio, aun su postrimería no será bendita.
22 Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
No digas, yo me vengaré; espera á Jehová, y él te salvará.
23 Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
Abominación son á Jehová las pesas dobles; y el peso falso no es bueno.
24 Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
De Jehová son los pasos del hombre: ¿cómo pues entenderá el hombre su camino?
25 Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
Lazo es al hombre el devorar lo santo, y andar pesquisando después de los votos.
26 Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
El rey sabio esparce los impíos, y sobre ellos hace tornar la rueda.
27 Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
Candela de Jehová es el alma del hombre, que escudriña lo secreto del vientre.
28 Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
Misericordia y verdad guardan al rey; y con clemencia sustenta su trono.
29 Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
La gloria de los jóvenes es su fortaleza, y la hermosura de los viejos la vejez.
30 Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.
Las señales de las heridas son medicina para lo malo: y las llagas [llegan] á lo más secreto del vientre.

< Miyambo 20 >