< Miyambo 20 >

1 Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
شراب انسان را به کارهای احمقانه وا می‌دارد و مشروب باعث عربده‌کشی می‌شود؛ چه نادانند کسانی که خود را اسیر مشروب می‌کنند.
2 Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
غضب پادشاه همچون غرش شیر است. هر که خشم او را برانگیزاند جان خود را به خطر می‌اندازد.
3 Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
اجتناب از نزاع برای شخص، عزت می‌آورد. فقط اشخاص نادان نزاع به پا می‌کنند.
4 Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
آدم تنبل به موقع زمینش را شخم نمی‌زند، پس در هنگام برداشت محصول هر چه می‌گردد چیزی نمی‌یابد.
5 Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
پند نیکو در اعماق دل مشورت دهنده مانند آب در ته چاه است و شخص فهمیده آن را بیرون می‌کشد.
6 Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
بسیارند کسانی که ادعا می‌کنند خوب و باوفا هستند، ولی کیست که بتواند شخص واقعاً باوفایی پیدا کند؟
7 Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
فرزندان شخص امین و درستکار در زندگی سعادتمند خواهند شد.
8 Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
پادشاهی که بر مسند قضاوت می‌نشیند به دقت جوانب امر را می‌سنجد و حق را از باطل تشخیص می‌دهد.
9 Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
کیست که بتواند بگوید: «دل خود را پاک نگه داشته‌ام و از گناه مبرا هستم.»
10 Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
خداوند از اشخاصی که در داد و ستد از وزنه‌ها و پیمانه‌های نادرست استفاده می‌کنند متنفر است.
11 Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
حتی کودک را می‌توان از طرز رفتارش شناخت و فهمید که آنچه انجام می‌دهد پاک و درست است یا نه.
12 Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
گوش شنوا و چشم بینا، هر دو بخشش خداوند هستند.
13 Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
اگر خواب را دوست داشته باشی فقیر می‌شوی؛ پس بیدار بمان تا سیر شوی.
14 Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
خریدار به جنس نگاه می‌کند و می‌گوید: «بد است!» اما بعد از خرید، از آن تعریف می‌کند.
15 Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
سخنان حکیمانه گرانبهاتر از طلا و نادرتر از جواهر است.
16 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
از کسی که نزد تو ضامن شخص غریبی می‌شود گرو بگیر.
17 Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
نانی که از راه کلاهبرداری به دست می‌آید لذیذ است، اما سرانجام کام را تلخ می‌کند.
18 Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
نقشه‌هایت را بدون مشورت با دیگران عملی نکن و بدون تدبیر به جنگ نرو.
19 Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
آدم سخن‌چین رازها را فاش می‌کند، پس با چنین شخصی معاشرت نکن.
20 Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
چراغ زندگی کسی که پدر و مادر خود را لعنت کند، خاموش خواهد شد.
21 Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
مالی که آسان به دست آمده باشد برکتی نخواهد داشت.
22 Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
بدی را با بدی تلافی نکن، بلکه منتظر باش تا خداوند عمل کند.
23 Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
خداوند از اشخاصی که در داد و ستد از ترازو و سنگهای نادرست استفاده می‌کنند متنفر است.
24 Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
خداوند راه زندگی ما را تعیین می‌کند، پس انسان چگونه می‌تواند بفهمد زندگی او به کجا ختم می‌شود؟
25 Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
هرگز نسنجیده قولی به خداوند نده، زیرا ممکن است گرفتار شوی.
26 Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
پادشاه دانا شریران را تشخیص می‌دهد و آنها را به شدت مجازات می‌کند.
27 Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
وجدان انسان به منزلهٔ چراغ خداوند است که تمام انگیزه‌های پنهانی او را آشکار می‌سازد.
28 Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
هرگاه پادشاهی مهربان و امین باشد، سلطنتش از محبت پایدار می‌ماند.
29 Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
شکوه جوانان، قوت ایشان است و عزت پیران، تجربه ایشان.
30 Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.
تنبیه برای بدن دردناک است اما دل را از بدی پاک می‌کند.

< Miyambo 20 >