< Miyambo 20 >
1 Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
Vinen er en spotter, sterk drikk volder støi, og hver den som raver av den, blir ikke vis.
2 Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
Den redsel en konge vekker, er som løvens brøl; den som gjør ham vred, spiller sitt liv.
3 Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
Det er en ære for en mann at han holder sig borte fra trette, men enhver dåre viser tenner.
4 Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
Om vinteren vil den late ikke pløie, derfor søker han forgjeves efter grøde om høsten.
5 Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
Tankene i en manns hjerte er et dypt vann, men en forstandig mann drar det op.
6 Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
Mange mennesker roper høit, hver om sin kjærlighet; men hvem finner vel en trofast mann?
7 Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
Den rettferdige vandrer i ustraffelighet; lykkelige er hans barn efter ham.
8 Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
En konge som sitter på sitt dommersete, sikter og skiller ut alt ondt med sine øine.
9 Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
Hvem kan si: Jeg har renset mitt hjerte, jeg er fri for min synd?
10 Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
To slags vektstener og to slags mål - begge deler er en vederstyggelighet for Herren.
11 Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
Allerede den unge gutt viser ved sine gjerninger om hans ferd vil bli ren og rett.
12 Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
Øret som hører, og øiet som ser - Herren har skapt dem begge to.
13 Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
Elsk ikke søvn, forat du ikke skal bli fattig! Lukk dine øine op, så får du brød nok å ete.
14 Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
Dårlig, dårlig! sier kjøperen; men når han går bort, roser han sig.
15 Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
Det er nok gull og perler i mengde, men kyndige leber er en kostelig ting.
16 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
Ta hans klær, han har gått i borgen for en annen, og ta pant av ham for fremmedes skyld!
17 Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
Brød vunnet ved svik smaker mannen søtt, men siden blir hans munn full av småsten.
18 Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
Planer får fremgang ved rådslagning; søk veiledning også når du fører krig!
19 Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
Den som går omkring som baktaler, åpenbarer hemmeligheter, og med den som er åpenmunnet, skal du ikke ha noget å gjøre.
20 Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
Den som banner sin far og sin mor, hans lampe skal slukne i belgmørke.
21 Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
En arv som en fra først av har revet til sig, blir til sist uten velsignelse.
22 Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
Si ikke: Jeg vil gjengjelde med ondt! Bi på Herren, og han skal frelse dig!
23 Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
To slags vektstener er en vederstyggelighet for Herren, og falsk vekt er noget ondt.
24 Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
Herren styrer mannens skritt; hvorledes skulde et menneske skjønne sin vei?
25 Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
Det er farlig for et menneske at han i tankeløshet vier noget til Gud og først bakefter overveier sine løfter.
26 Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
En vis konge skiller ut de ugudelige og lar hjulet gå over dem.
27 Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
Menneskets ånd er en Herrens lampe; den ransaker alle lønnkammerne i hans indre.
28 Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
Miskunnhet og sanndruhet er en vakt om kongen, og han støtter sin trone ved miskunnhet.
29 Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
De unges pryd er deres kraft, og de gamles ære er de grå hår.
30 Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.
Et tuktemiddel for de onde er buler og sår og slag, som trenger inn i hjertets indre.