< Miyambo 20 >

1 Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
Moqueur est le vin, bruyante la boisson fermentée: qui s’en laisse troubler manque de sens.
2 Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
La terreur qu’inspire le roi est comme le rugissement du lion; qui l’irrite compromet sa vie.
3 Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
C’Est l’honneur de l’homme de se tenir loin des disputes; mais tout sot s’y jette à corps perdu.
4 Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
Sous prétexte de froid le paresseux s’abstient de labourer; la moisson venue, il cherche et ne trouve rien.
5 Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
Telles des eaux profondes, les idées abondent dans le cœur humain: l’homme avisé sait y puiser.
6 Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
Nombre d’hommes sont vantés pour leur bonté; mais qui trouvera un homme d’une entière loyauté?
7 Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
Le juste marche dans son intégrité; heureux, ses enfants après lui!
8 Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
Le roi, assis sur le trône de justice, disperse par ses regards tous les malfaiteurs.
9 Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
Qui osera dire: "J’Ai débarrassé mon cœur de toute tache, je suis purifié de mes péchés?"
10 Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
Deux poids et deux mesures sont également en horreur à l’Eternel.
11 Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
Déjà le jeune homme se révèle par ses actes, laissant deviner si son œuvre sera pure et droite.
12 Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
L’Oreille qui entend, l’œil qui voit, l’Eternel les a faits tous deux.
13 Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
N’Aime pas trop le sommeil, sous peine de t’appauvrir; aie les yeux ouverts et tu auras du pain en abondance.
14 Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
"Mauvais, mauvais!" dit l’acheteur: il se retire et s’applaudit du marché.
15 Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
Il existe de l’or, une quantité de perles fines; mais la parure précieuse entre toutes, ce sont des lèvres intelligentes.
16 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
Quelqu’un s’est-il porté garant pour un étranger, saisis son vêtement; s’il cautionne une inconnue, nantis-toi de son gage.
17 Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
Le pain dû au mensonge peut être agréable à l’homme; finalement, sa bouche est pleine de gravier.
18 Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
Que tes résolutions soient fondées sur la réflexion; fais la guerre suivant un plan habile.
19 Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
Qui colporte des commérages trahit des secrets; n’aie aucun rapport avec le bavard imprudent.
20 Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
Si quelqu’un maudit père et mère, que son flambeau soit comme un lumignon fumeux dans d’épaisses ténèbres!
21 Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
Un héritage souillé dans sa source ne saurait être béni dans la suite.
22 Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
Ne dis pas: "Je veux rendre le mal!" Espère en Dieu, il te prêtera secours.
23 Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
Deux poids sont en horreur à l’Eternel; des balances trompeuses, quelle détestable chose!
24 Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
Les pas de l’homme sont dirigés par Dieu; mais combien l’homme doit considérer sa voie!
25 Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
L’Abus des choses saintes est un piège pour l’homme, comme de prodiguer les vœux.
26 Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
Un roi sage disperse les méchants et fait passer la roue sur eux.
27 Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
L’Âme de l’homme est un flambeau divin, qui promène ses lueurs dans les replis du cœur.
28 Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
La bonté et la vérité protègent le roi; le soutien de son trône, c’est l’amour.
29 Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
La vigueur est la gloire de la jeunesse, les cheveux blancs la parure de la vieillesse.
30 Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.
De cuisantes blessures sont comme un onguent pour le méchant, ainsi que des coups qui retentissent jusqu’au fond de l’être.

< Miyambo 20 >