< Miyambo 20 >
1 Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
Wiyn is a letcherouse thing and drunkenesse is ful of noise; who euere delitith in these, schal not be wijs.
2 Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
As the roryng of a lioun, so and the drede of the kyng; he that territh hym to ire, synneth ayens his owne lijf.
3 Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
It is onour to a man that departith hym silf fro stryuyngis; but fonned men ben medlid with dispisyngis.
4 Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
A slow man nolde ere for coold; therfor he schal begge in somer, and me schal not yyue to hym.
5 Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
As deep watir, so counsel is in the herte of a man; but a wijs man schal drawe it out.
6 Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
Many men ben clepid merciful; but who schal fynde a feithful man?
7 Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
Forsothe a iust man that goith in his simplenesse, schal leeue blessid sones aftir hym.
8 Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
A king that sittith in the seete of doom, distrieth al yuel bi his lokyng.
9 Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
Who may seie, Myn herte is clene; Y am clene of synne?
10 Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
A weiyte and a weiyte, a mesure and a mesure, euer eithir is abhomynable at God.
11 Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
A child is vndurstondun bi hise studies, yf his werkis ben riytful and cleene.
12 Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
An eere heringe, and an iye seynge, God made euere eithir.
13 Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
Nyle thou loue sleep, lest nedynesse oppresse thee; opene thin iyen, and be thou fillid with looues.
14 Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
Ech biere seith, It is yuel, it is yuel; and whanne he hath go awey, thanne he schal haue glorie.
15 Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
Gold, and the multitude of iemmes, and a preciouse vessel, ben the lippis of kunnyng.
16 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
Take thou awei the cloth of hym, that was borewe of an othere man; and for straungeris take thou awei a wed fro hym.
17 Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
The breed of a leesing is sweet to a man; and aftirward his mouth schal be fillid with rikenyng.
18 Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
Thouytis ben maad strong bi counselis; and bateils schulen be tretid bi gouernals.
19 Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
Be thou not medlid with him that schewith pryuetees, and goith gylefulli, and alargith hise lippis.
20 Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
The liyt of hym that cursith his fadir and modir, schal be quenchid in the myddis of derknessis.
21 Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
Eritage to which me haastith in the bigynnyng, schal wante blessing in the laste tyme.
22 Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
Seie thou not, Y schal yelde yuel for yuel; abide thou the Lord, and he schal delyuere thee.
23 Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
Abhomynacioun at God is weiyte and weiyte; a gileful balaunce is not good.
24 Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
The steppis of man ben dressid of the Lord; who forsothe of men mai vndurstonde his weie?
25 Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
Falling of man is to make auow to seyntis, and aftirward to withdrawe the vowis.
26 Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
A wijs kyng scaterith wickid men; and bowith a bouwe of victorie ouer hem.
27 Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
The lanterne of the Lord is the spirit of man, that sekith out alle the priuetees of the wombe.
28 Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
Merci and treuthe kepen a kyng; and his trone is maad strong bi mekenesse.
29 Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
The ful out ioiyng of yonge men is the strengthe of hem; and the dignyte of elde men is hoornesse.
30 Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.
The wannesse of wounde schal wipe aweie yuels, and woundis in the priuyere thingis of the wombe.