< Miyambo 20 >

1 Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
Wine is, a scoffer, and strong drink, a brawler, every one therefore who erreth therein, is unwise.
2 Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
The growl as of a young lion, is the dread inspired by a king, he that provoketh him, endangereth his own life.
3 Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
Honour, hath the man who sitteth away from strife, but, any fool, may break through.
4 Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
By reason of the autumn, a sluggard will not plough, therefore shall he beg in harvest, and there be nothing.
5 Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
Deep water, is counsel in a man’s heart, but, a man of understanding, will draw it out.
6 Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
A kind man one may call, a great man, —but, a faithful man, who can find?
7 Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
As for a righteous man, walking in his integrity, how happy are his children after him!
8 Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
A king sitting on the throne of judgment, scattereth, with his eyes, all wrong.
9 Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
Who can say, I have cleansed my heart, I am pure from my sin?
10 Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
Divers weights, and divers measures, an abomination to Yahweh, are they, both.
11 Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
Even, by his doings, doth a youth make himself known, whether, pure and upright, be his work.
12 Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
The hearing ear, and the seeing eye, Yahweh hath made them, both.
13 Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
Do not love sleep, lest thou come to poverty, open thine eyes, be satisfied with bread.
14 Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
Bad! bad! saith the buyer, but, going his way, then, he boasteth.
15 Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
There are gold, and an abundance of corals, but, precious jewels, are the lips of knowledge.
16 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
Take his garment who is pledge for a stranger, —then, for a woman unknown, accept him as surety.
17 Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
Sweet to a man, may be the bread of falsehood, but, afterward, shall his mouth be filled with gravel.
18 Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
Plans—by counsel, shalt thou establish, and, with concerted measures, make thou war.
19 Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
A revealer of secrets, is one who goeth about talebearing, therefore, with him who openeth his lips, shalt thou not have fellowship.
20 Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
Whoso revileth his father or his mother, his lamp shall be put out in deep darkness.
21 Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
An inheritance hastily gotten at the beginning, the latter end thereof, shall not bring blessing.
22 Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
Do not say, I will requite wrong! Wait thou for Yahweh that he may save thee.
23 Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
An abomination to Yahweh, are divers weights, and, deceptive balances, are not good.
24 Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
From Yahweh, are a man’s steps, a son of earth, then—how can he discern his way?
25 Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
It is a snare to a man, that he should rashly cry Holy! and, after making vows, to reflect!
26 Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
A wise king, winnoweth out the lawless, when he hath turned over them the wheel.
27 Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
The lamp of Yahweh, is the spirit of a son of earth, searching all the chambers of the inner man.
28 Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
Lovingkindness and faithfulness, will guard a king, —therefore should he support, with lovingkindness, his throne.
29 Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
The beauty of young men, is their strength, and, the ornament of old men, a hoary head.
30 Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.
Blows that cut in, cleanse away wickedness, and, smitings, [enter] the chambers of the inner man.

< Miyambo 20 >