< Miyambo 20 >

1 Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
Wine is a mocker, strong drink a brawler; and whosoever erreth thereby is not wise.
2 Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
The terror of a king is as the roaring of a lion: he that provoketh him to anger sinneth [against] his own life.
3 Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
It is an honour for a man to keep aloof from strife: but every fool will be quarrelling.
4 Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
The slothful will not plow by reason of the winter; therefore he shall beg in harvest, and have nothing.
5 Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
Counsel in the heart of man is [like] deep water; but a man of understanding will draw it out.
6 Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
Most men wilt proclaim every one his own kindness: but a faithful man who can find?
7 Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
A just man that walketh in his integrity, blessed are his children after him.
8 Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
A king that sitteth on the throne of judgment scattereth away all evil with his eyes.
9 Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
Who can say, I have made my heart clean, I am pure from my sin?
10 Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
Divers weights, and divers measures, both of them alike are an abomination to the LORD.
11 Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
Even a child maketh himself known by his doings, whether his work be pure, and whether it be right.
12 Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
The hearing ear, and the seeing eye, the LORD hath made even both of them.
13 Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
Love not sleep, lest thou come to poverty; open thine eyes, [and] thou shalt be satisfied with bread.
14 Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
It is naught, it is naught, saith the buyer: but when he is gone his way, then he boasteth.
15 Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
There is gold, and abundance of rubies: but the lips of knowledge are a precious jewel.
16 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
Take his garment that is surety for a stranger; and hold him in pledge [that is surety] for strangers.
17 Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
Bread of falsehood is sweet to a man; but afterwards his mouth shall be filled with gravel.
18 Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
Every purpose is established by counsel: and by wise guidance make thou war,
19 Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
He that goeth about as a talebearer revealeth secrets: therefore meddle not with him that openeth wide his lips.
20 Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
Whoso curseth his father or his mother, his lamp shall be put out in the blackest darkness.
21 Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
An inheritance [may be] gotten hastily at the beginning; but the end thereof shall not be blessed.
22 Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
Say not thou, I will recompense evil: wait on the LORD, and he shall save thee.
23 Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
Divers weights are an abomination to the LORD; and a false balance is not good.
24 Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
A man’s goings are of the LORD; how then can man understand his way?
25 Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
It is a snare to a man rashly to say, [It is] holy, and after vows to make inquiry.
26 Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
A wise king winnoweth the wicked, and bringeth the [threshing] wheel over them.
27 Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
The spirit of man is the lamp of the LORD, searching all the innermost parts of the belly.
28 Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
Mercy and truth preserve the king: and his throne is upholden by mercy.
29 Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
The glory of young men is their strength: and the beauty of old men is the hoary head.
30 Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.
Stripes that wound cleanse away evil: and strokes [reach] the innermost parts of the belly.

< Miyambo 20 >