< Miyambo 20 >
1 Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
Wine is an intemperate thing, and strong drink full of violence: but every fool is entangled with them.
2 Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
The threat of a king differs not from the rage of a lion; and he that provokes him sins against his own soul.
3 Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
[It is] a glory to a man to turn aside from railing; but every fool is entangled with such matters.
4 Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
A sluggard when reproached is not ashamed: so also he who borrows corn in harvest.
5 Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
Counsel in a man's heart is deep water; but a prudent man will draw it out.
6 Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
A man is valuable, and a merciful man precious: but [it is] hard to find a faithful man.
7 Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
He that walks blameless in justice, shall leave his children blessed.
8 Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
Whenever a righteous king sits on the throne, no evil thing can stand before his presence.
9 Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
Who will boast that he has a pure heart? or who will boldly say that he is pure from sins?
10 Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
A large and small weight, and various measures, are even both of them unclean before the Lord; and [so is] he that makes them.
11 Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
A youth [when in company] with a godly man, will be restrained in his devices, and [then] his way will be straight.
12 Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
The ear hears, and the eye sees: even both of them are the Lord's work.
13 Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
Love not to speak ill, lest you be cut off: open your eyes, and be filled with bread.
14 Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
15 Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
16 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
17 Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
18 Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
19 Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
20 Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
The lamp of him that reviles father or mother shall be put out, and his eyeballs shall see darkness.
21 Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
A portion hastily gotten at first shall not be blessed in the end.
22 Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
Say not, I will avenge myself on my enemy; but wait on the Lord, that he may help you.
23 Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
A double weight is an abomination to the Lord; and a deceitful balance is not good in his sight.
24 Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
A man's goings are directed of the Lord: how then can a mortal understand his ways?
25 Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
It is a snare to a man hastily to consecrate some of his own property: for [in that case] repentance comes after vowing.
26 Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
A wise king utterly crushes the ungodly, and will bring a wheel upon them.
27 Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
The spirit of man is a light of the Lord, who searches the inmost parts of the belly.
28 Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
Mercy and truth are a guard to a king, and will surround his throne with righteousness.
29 Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
Wisdom is an ornament to young men; and grey [hairs] are the glory of old men.
30 Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.
Bruises and contusions befall bad men; and plagues [shall come] in the inward parts of [their] belly.