< Miyambo 20 >
1 Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
Vin er en Spotter, stærk Drik en Larmer, og hver som raver deraf, bliver ikke viis.
2 Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
Den Forfærdelse, en Konge vækker, er som en ung Løves Brølen; den, som fortørner ham, synder imod sit Liv.
3 Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
Det er en Ære for en Mand at blive fra Trætte, men hver Daare vælter sig ind i den.
4 Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
Fordi det er Vinter, vil den lade ikke pløje; om Høsten vil han søge, og der er intet.
5 Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
Raad i en Mands Hjerte er dybt Vand, men en forstandig Mand drager det op.
6 Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
Mange Mennesker udraabe hver sin Kærlighed; men hvo finder en trofast Mand?
7 Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
Den, som vandrer frem i sin Oprigtighed, er retfærdig; lyksalige ere hans Børn efter ham.
8 Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
En Konge, som sidder paa Domstolen, udskiller alle onde med sine Øjne.
9 Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
Hvo kan sige: Jeg har renset mit Hjerte; jeg er ren for min Synd?
10 Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
To Slags Vægt og to Slags Efa, de ere begge en Vederstyggelighed for Herren.
11 Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
Ogsaa af sine Gerninger kendes den unge, om han er ren, og om hans Gerning er ret.
12 Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
Et Øre, som hører, og et Øje, som ser, ogsaa dem begge har Herren gjort.
13 Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
Elsk ikke Søvn, at du ikke skal blive fattig; slaa dine Øjne op, saa skal du mættes af Brød.
14 Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
Det er slet! det er slet! siger Køberen; men naar han gaar bort, da roser han sig.
15 Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
Der er Guld og mange Perler til; men Kundskabs Læber ere et dyrebart Kar.
16 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
Naar en gaar i Borgen for en fremmed, saa tag hans Klæder; og tag Pant af ham, naar det er for den ubekendte.
17 Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
Brød, tjent ved Bedrag, smager en Mand vel; men siden bliver hans Mund fuld af Grus.
18 Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
Beslutninger efter Raadslagning bestaa; før da Krig efter fornuftig Ledelse!
19 Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
Den, der gaar om som en Bagvadsker, aabenbarer Hemmeligheder; og indlad dig ikke med den, som er aabenmundet.
20 Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
Hvo som bander sin Fader eller sin Moder, hans Lampe skal udslukkes midt i Mørket.
21 Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
Den Arv, som man i Førstningen higer efter, den skal ikke velsignes paa det sidste.
22 Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
Sig ikke: Jeg vil betale ondt; bi efter Herren, og han skal frelse dig.
23 Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
To Slags Vægt er en Vederstyggelighed for Herren, og falske Vægtskaaler ere ikke gode.
24 Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
En Mands Gang er at Herren, og hvad forstaar et Menneske sig paa sin Vej?
25 Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
Det er Mennesket en Snare ubesindigt at sige: „Helligt!‟ og først efter Løfterne betænke det.
26 Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
En viis Konge udskiller de ugudelige og lader Hjulet gaa over dem.
27 Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
Menneskens Aand er en Lampe fra Herren; den ransager alle Lønkamre i hans Indre.
28 Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
Miskundhed og Sandhed bevare en Konge, og han støtter sin Trone ved Miskundhed.
29 Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
En Pryd for de unge er deres Kraft, og et Smykke for de gamle ere de graa Haar.
30 Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.
En Salvelse for den onde ere Striber af Saar og Slag, der trænge dybt ind i hans Krop.