< Miyambo 20 >

1 Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
Vino je podsmjevač, žestoko piće bukač, i tko se njima odaje neće steći mudrosti.
2 Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
Kraljev je gnjev kao rika lavlja: tko ga izaziva, griješi protiv sebe samog.
3 Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
Čast je čovjeku ustegnuti se od raspre, a tko je bezuman počinje svađu.
4 Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
Lijenčina u jesen ne ore: u doba žetve on traži, i ništa nema.
5 Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
Savjet je u srcu čovječjem voda duboka i razuman će je čovjek iscrpsti.
6 Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
Mnogi se naziva dobrim čovjekom, ali tko će naći vjerna čovjeka?
7 Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
Pravednik hodi u bezazlenosti svojoj: blago sinovima njegovim poslije njega!
8 Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
Kralj koji sjedi na stolici sudačkoj istražuje svako zlo svojim očima.
9 Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
Tko može reći: “Očistih srce svoje, oprah se od grijeha svoga?”
10 Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
Dvojaki utezi i dvojaka mjera mrski su Jahvi podjednako.
11 Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
I dijete se poznaje po onome što čini, je li čisto i pravedno djelo njegovo.
12 Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
I uho koje čuje i oko koje vidi, oboje je Jahve načinio.
13 Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
Ne ljubi sna, da ne osiromašiš; otvori oči svoje i nasitit ćeš se kruha.
14 Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
“Loše, loše”, govori kupac, a kad ode, hvali se dobrom kupovinom.
15 Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
Ima zlata i mnogih bisera, ali su mudre usne najdragocjeniji nakit.
16 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
Uzmi haljinu onomu tko je jamčio za drugoga; oplijeni njega umjesto tuđinca.
17 Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
Sladak je čovjeku kruh prijevare, ali mu se usta poslije napune pijeskom.
18 Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
Naumi se provode savjetom: zato dobro razmisli pa vodi boj!
19 Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
Tko okolo kleveće, otkriva tajne: zato se ne miješaj s onim komu su usne uvijek otvorene.
20 Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
Tko kune oca svoga i majku svoju svjetiljka mu se gasi usred tmine.
21 Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
Od početka brzo stečeno imanje na koncu nije blagoslovljeno.
22 Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
Nemoj govoriti: “Osvetit ću se za zlo”; čekaj Jahvu, i on će te spasiti.
23 Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
Mrski su Jahvi dvojaki utezi, i kriva mjera ne valja.
24 Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
Od Jahve su koraci čovječji, i kako da čovjek razumije svoj put?
25 Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
Zamka je čovjeku nesmotreno reći: “Ovo je sveto”, a poslije promišljati što je zavjetovao.
26 Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
Mudar kralj umije izlučiti opake i stavlja ih pod točkove.
27 Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
Svjetiljka je Gospodnja duh čovječji: ona istražuje sve do dna utrobe.
28 Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
Dobrota i vjernost čuvaju kralja, jer dobrotom utvrđuje prijestol svoj.
29 Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
Ljepota je mladićima njihova snaga, a starcima je ures sijeda kosa.
30 Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.
Krvave masnice očiste zlo i udarci pročiste odaje utrobe.

< Miyambo 20 >