< Miyambo 20 >
1 Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
清酒令人輕狂,醇酒使人發瘋;凡沉溺於酒的,必不是明智人。
2 Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
君王震怒,有如獅子的咆哮;觸怒他的,危害自己的性命。
3 Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
平息爭端,是人的光榮;凡是愚人,都喜愛爭論。
4 Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
懶惰人一寒冷,便不耕作;收獲之時,他必一無所獲。
5 Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
人心的謀略,有如深水,唯有聰明人,纔能汲取。
6 Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
自命為仁者,比比皆是;但有誰找到忠貞的人﹖
7 Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
正義的人,必然為人正直;他的後代子孫,必然有福。
8 Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
君王高坐在判座上,所有邪惡一目了然。
9 Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
有誰能說:「我保持了心靈的潔淨,我是純潔無罪的﹖」
10 Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
不同的衡量,不同的升斗:二者皆為上主同樣厭惡。
11 Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
孩童的行為,潔淨正執直與否,由他的舉動便可認出。
12 Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
能聽的耳朵,能看的眼睛:二者皆為上主所造。
13 Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
不要貪睡眠,免得你受窮;兩眼睜開,纔能得飽食。
14 Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
顧客常說:「不好,不好! 」但一離去,讚不絕口。
15 Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
雖有大批黃金寶石,但最寶貴的,還是明智的唇舌。
16 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
誰為外方人作保,拿去他的衣服;誰為異邦人作保,以他本人作質。
17 Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
騙來的食物頗覺香甜,事後口中卻滿是砂礫。
18 Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
運籌帷幄,必先要商討;進行戰事,必該憑智謀。
19 Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
遊蕩閒談的,必洩露秘密;張口饒舌的,別與他交結。
20 Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
凡是辱罵自己父母的人,他的燈必在幽暗中熄滅。
21 Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
起初容易得來的財物,最後也不會得到祝福。
22 Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
你切不可說:「我以惡報惡;」應信賴上主,他必拯救你。
23 Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
不同的衡量,為上主所惡;不同的天秤,實屬不道德。
24 Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
世人的腳步,由上主支配;人那能了解自己的道路﹖
25 Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
人若冒然說「聖,」許願後纔反省,這是自投羅網。
26 Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
智慧的君王簸揚惡人,且用車輪來壓軋他們。
27 Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
人的靈魂是天主的燈,探照肺腑的一切隱密。
28 Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
仁愛和忠誠,是君王的保障;他的寶座,是賴慈愛而支撐。
29 Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
少年人的光榮,在於他們的魄力;老年人的榮耀,在於他們的白髮。
30 Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.
見傷的鞭打能清除邪惡,杖擊能觸及肺腑的深處。