< Miyambo 20 >

1 Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
Misurtui ing thlang thekhanaak pe nawh, zuu ing awipungnaak coeng sak hy.
2 Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
Sangpahrang ak kawsonaak taw samthyn a kaawk ing myih nawh, kaw ak so sak taw amah a hqingnaak ak khawng ni.
3 Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
Kawsonaak ak qei thlang ing kyihcahnaak hu kawm saw, cehlai thlakqaw ingtaw hqo hu hy.
4 Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
Thlang thakdam ing khaw a dingawh lai a thawl ngak nawh; cedawngawh caang ah huiawh ai thoeh kawm saw, ikawawm am ta kaw.
5 Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
Kawlung khuiawh cainaak taw tui amyihna dung hlai hy, simnaak ak ta thlang ing ni ik-oeih a coeng sak hy.
6 Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
Thlak ypawmna kqawn qu mai kawm uh, ak ypawm tang unu ak awm?
7 Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
Thlakdyng, khawkpoek khawkhan thainaak ak ta a cakhqi taw thlang zoseenkhqi ni.
8 Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
Awitlyknaak awh Sangpahrang ing awi ak tlyk awh, a mik ing theem amak leek boeih ce khqaa ing zah amyihna zaap boeih hy.
9 Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
“Kak kawlung ciim sak nyng, thawlhnaak awhkawng ciimcaih nyng,” tinawh uing ak kqawn thai?
10 Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
Tahnaak amak thym ingkaw tehnaak amak thym boeih Bawipa ing tyih qawi haih hy.
11 Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
Nasen awm a bibi ing ak thym ak thawlh dang sak hy.
12 Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
Zaaknaak haa ingkaw huhnaak mik ve Bawipa ing ni a sai qawi haih.
13 Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
Ih koeh lungna khawdeng kawp ti; hqak nawh meet lah awklek ainaa ta kawp ti.
14 Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
Them ak thlaikung ing them ak thlaihawh “Am leek hy, am leek hy,” tinawh, ang voei huna a them thlaihawh oequ hy.
15 Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
Sui awm nawh, cak phu tlo awm awm moe, cyihnaak awi ak kqawn hui taw lung phu tlo soeih ing myih hy.
16 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
Thlangchang asyng naak ham ak dyihpyi-kung ingkaw nukche ak dyihpyikung ing a hii ce hawlh seh.
17 Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
Quuk buh ang hypna ai ve thlang ing tui sak hy, cehlai a huna am kha ce lungqiit ing be kaw.
18 Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
Thlang doet nawh ik-oeih cainaak ta. Ak leekna cai hqeet nawh ceemqal ce tlyk.
19 Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
Thlang awihpung khawlakawh ak van ing awihyp ce pho sak hy; Ceamyihna awmsaw awi ak pung thlang ce koeh pyi na.
20 Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
A nu mai aw, a pa mai aw qun ak khy pek taw, thanlung ak hyp huiawh a maihchoei him pekna awm kaw.
21 Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
Ak cykawh ang tawnna huh qo cetaw a huna zoseetnaak na awm kaw.
22 Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
“Thawlh thung lah vang,” koeh ti, Khawsa ce qeh cang nawh, anih ing ni loet sak kaw.
23 Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
Tahnaak amak thym taw Bawipa mikhuhawh tuih kawi ni, amak thym tehnaak awm am leek hy.
24 Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
Thlanghqing a khawkhannaak Bawipa ing a hqui ni, cekkaana thlanghqing ing ikawmyihna a sim hly thai?
25 Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
Poek kaana hqingtawnnaak ing Khawsa them pek ingkaw awikam coengawh hu ak nawng tlaih taw amah ham thang ak dun khoeng ak thlang ni.
26 Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
Sangpahrang ak cyi ing thlakche ce hqimqa nawh awideng hy.
27 Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
Thlanghqing kak kawlung taw Bawipa a maihchoeina awm nawh, kawlung khui a dungnaak dy coei pheng thai hy.
28 Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
Lungnaak ingkaw awitak ing sangpahrang ce syng sak nawh; lungnaak ingawh ang ngawih-naak ce cak sak hy.
29 Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
Cacoen a boeimangnaak taw ak thamahnaak ni, Pacawng a dawnaak taw a lumkqawk sampainaak ni.
30 Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.
Mynmaa kawlawknaak ing boeibaai caih sak nawh, vyyknaak ing kawlung ak khui dy ciim sak hy.

< Miyambo 20 >