< Miyambo 2 >
1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
I oƣlum, ǝgǝr sɵzlirimni ⱪobul ⱪilsang, Nǝsiⱨǝtlirimni ⱪǝlbinggǝ püksǝng,
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
Əgǝrdǝ danaliⱪⱪa ⱪulaⱪ salsang, Yoruⱪluⱪⱪa erixixkǝ kɵngül bǝrsǝng,
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
Əgǝr ǝⱪil-parasǝtkǝ tǝxna bolup iltija ⱪilsang, Yoruⱪluⱪⱪa erixix üqün yuⱪiri awazda yelinsang,
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
Əgǝr kümüxkǝ intilgǝndǝk intilsǝng, Yoxurun gɵⱨǝrni izdigǝndǝk izdisǝng,
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
Undaⱪta Pǝrwǝrdigardin [ⱨǝⱪiⱪiy] ⱪorⱪuxni bilidiƣan bolisǝn, Wǝ sanga Hudani tonux nesip bolidu.
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
Qünki Pǝrwǝrdigar danaliⱪ bǝrgüqidur; Uning aƣzidin bilim bilǝn yoruⱪluⱪ qiⱪidu.
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
U durus yaxawatⱪanlar üqün mol ⱨekmǝt tǝyyarlap ⱪoyƣandur, U wijdanliⱪ adǝmlǝr üqün ⱪalⱪandur.
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
U adilliⱪ ⱪilƣuqilarning yollirini asraydu, Ihlasmǝn bǝndilirining yolini ⱪoƣdaydu.
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
U qaƣda ⱨǝⱪⱪaniyliⱪ, adilliⱪ wǝ durusluⱪni, Xundaⱪla ⱨǝrⱪandaⱪ güzǝl yolni qüxinidiƣan bolisǝn.
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
Danaliⱪ ⱪǝlbinggǝ kirixi bilǝnla, Bilim kɵnglünggǝ yeⱪixi bilǝnla,
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
Pǝm-parasǝt seni ⱪoƣdaydu, Yoruⱪluⱪ seni saⱪlaydu.
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
Ular seni yaman yoldin, Tili zǝⱨǝr adǝmlǝrdin ⱪutⱪuzidu;
13 amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
Yǝni toƣra yoldin qǝtnigǝnlǝrdin, Ⱪarangƣu yollarda mangidiƣanlardin,
14 amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
Rǝzillik ⱪilixni ⱨuzur kɵridiƣanlardin, Yamanliⱪning ziyanlirini huxalliⱪ dǝp bilidiƣanlardin,
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
Yǝni ǝgri yollarda mangidiƣanlardin, Ⱪingƣir yolda mangidiƣanlardin ⱪutⱪuzidu.
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
[Danaliⱪ] seni buzuⱪ ayaldin, Yǝni xirin sɵzlǝr bilǝn azdurmaⱪqi bolƣan namǝⱨrǝm ayallardin ⱪutⱪuzidu.
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
[Bundaⱪ ayallar] yax waⱪtida tǝgkǝn jorisini taxlap, Huda aldidiki nikaⱨ ⱪǝsimini untuƣan wapasizlardindur.
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
Uning ɵyigǝ baridiƣan yol ɵlümgǝ apiridiƣan yoldur, Uning mangidiƣan yolliri adǝmni ǝrwaⱨlar makaniƣa baxlaydu.
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
Uning ⱪexiƣa barƣanlarning birimu ⱪaytip kǝlgini yoⱪ, Ulardin birimu ⱨayatliⱪ yolliriƣa erixkini yoⱪ.
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
[Xularni qüxǝnsǝng] yahxilarning yolida mangisǝn, Ⱨǝⱪⱪaniylarning yollirini tutisǝn.
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
Qünki durus adǝm zeminda yaxap ⱪalalaydu, Mukǝmmǝl kixi bu yǝrdǝ makanlixalaydu.
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
Lekin rǝzillǝr zemindin üzüp taxlinidu, Wapasizlar uningdin yuluwetilidu.