< Miyambo 2 >

1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
Hijo mío, si aceptas mis palabras, Y guardas mis mandamientos dentro de ti,
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
Eres de oído atento a la sabiduría, E inclinas tu corazón a la inteligencia,
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
Si invocas a la prudencia, Y al entendimiento alzas tu voz,
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
Si la procuras como a la plata, Y la rebuscas como a tesoros escondidos,
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
Entonces entenderás el temor a Yavé, Y hallarás el conocimiento de ʼElohim.
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
Porque Yavé da la sabiduría. De su boca procede la ciencia y la inteligencia.
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
Él atesora el acierto para los hombres rectos, Es escudo al que anda en integridad.
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
Es el que guarda las sendas de la justicia, Y preserva el camino de sus santos.
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
Entonces entenderás la justicia y el derecho, La equidad y todo buen camino.
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
Cuando la sabiduría entre en tu corazón Y el conocimiento sea dulce a tu alma,
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
Te guardará la discreción. Te preservará la prudencia
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
Para librarte del camino malo Del hombre que habla cosas perversas,
13 amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
De los que abandonan los caminos rectos Para andar por sendas tenebrosas,
14 amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
De los que gozan haciendo el mal, Y se alegran en las perversidades del vicio,
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
Cuyas sendas son tortuosas, Y sus caminos extraviados.
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
Te librará de la mujer ajena, De la extraña que endulza sus palabras,
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
Que abandona al compañero de su juventud Y olvida el Pacto de su ʼElohim.
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
Su casa se inclina hacia la muerte, Sus sendas hacia el país de las sombras.
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
Cuantos entran en ella no regresan, Ni retoman los senderos de la vida.
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
Para que sigas el buen camino Y guardes los senderos del justo.
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
Porque los rectos vivirán en la tierra, Y los de limpio corazón permanecerán en ella.
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
Pero el perverso será cortado de la tierra, Y de ella serán desarraigados los transgresores.

< Miyambo 2 >