< Miyambo 2 >
1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
Filho meu, se aceitares as minhas palavras, e esconderes contigo os meus mandamentos,
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
Para fazeres atento à sabedoria o teu ouvido, e inclinares o teu coração ao entendimento,
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
E se clamares por entendimento, e por inteligência alçares a tua voz,
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
Se como a prata a buscares e como a tesouros escondidos a esquadrinhares,
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
Então entenderás o temor do Senhor, e acharás o conhecimento de Deus.
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
Porque o Senhor é o que dá a sabedoria: da sua boca é que sai o conhecimento e o entendimento.
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
Ele reserva a verdadeira sabedoria para os retos: escudo é para os que caminham na sinceridade.
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
Para que guardem as veredas do juízo: e ele o caminho dos seus santos conservará.
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
Então entenderás justiça, e juízo, e equidades, e todas as boas veredas,
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
Quando a sabedoria entrar no teu coração, e o conhecimento for suave à tua alma.
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
O bom siso te guardará e a inteligência te conservará;
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
Para te fazer escapar do mau caminho, e do homem que fala coisas perversas.
13 amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
Dos que deixam as veredas da retidão, para andarem pelos caminhos das trevas.
14 amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
Que se alegram de mal fazer, e folgam com as perversidades dos maus.
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
Cujas veredas são tortuosas e que se desviam nas suas carreiras,
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
Para te fazer escapar da mulher estranha, e da estrangeira que lisongeia com suas palavras.
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
Que deixa o guia da sua mocidade e se esquece do concerto do seu Deus.
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
Porque a sua casa se inclina para a morte, e as suas veredas para os defuntos.
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
Todos os que entrarem a ela não tornarão a sair, e não atinarão com as veredas da vida.
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
Para andares pelo caminho dos bons, e guardares as veredas dos justos.
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
Porque os retos habitarão a terra, e os sinceros permanecerão nela.
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
Mas os ímpios serão arrancados da terra, e os aleivosos serão dela exterminados.