< Miyambo 2 >

1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
Mwana na ngai, soki ondimi maloba na ngai mpe obateli kati na motema na yo mibeko na ngai;
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
soki opesi litoyi na yo na maloba ya bwanya mpe okabi motema na yo na makambo ya mayele;
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
soki obeleli mayele mpe ogangi epai ya bososoli;
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
soki oluki yango penza ndenge balukaka palata to bomengo oyo ebombama,
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
okososola solo soki kotosa Yawe elakisi nini mpe okozwa boyebi ya Nzambe.
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
Pamba te Yawe nde apesaka bwanya, mpe maloba ya monoko na Ye epesaka mayele mpe bososoli.
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
Abongiselaka bato ya sembo elonga mpe azali nguba ya bato oyo batambolaka na bosembo.
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
Pamba te abatelaka bayengebene mpe nzela ya bato oyo batosaka Ye.
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
Boye, okososola likambo nini ezali solo, alima, sembo: nzela nyonso oyo ememaka na bolamu.
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
Pamba te bwanya ekokota kati na motema na yo mpe boyebi ekosepelisa molimo na yo.
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
Bososoli ekobatela yo, mpe mayele ekobomba yo
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
mpo na kobikisa yo na nzela mabe, na moto oyo alobaka makambo ezanga tina,
13 amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
na bato oyo batikaka nzela ya sembo mpo na kolanda nzela ya molili,
14 amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
na bato oyo basepelaka kosala mabe, na bato oyo bazalaka na esengo ya kokota na bozindo ya mabe,
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
na bato oyo nzela na bango etengama-tengama mpe etamboli na bango etonda na mobulu.
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
Bwanya ekobikisa yo lisusu liboso ya mwasi mopaya, liboso ya mwasi oyo atonda na maloba ya sukali,
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
oyo akima mobali na ye ya bolenge mpe abosana boyokani oyo asalaki elongo na Nzambe na ye;
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
pamba te ndako na ye ememaka na kufa, mpe nzela na ye ememaka na mboka ya bakufi.
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
Moto moko te oyo akotaka epai na ye azongaka mpe amonaka lisusu nzela ya bomoi.
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
Boye, okotambola na nzela ya bato malamu mpe okolanda nzela ya bato ya sembo.
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
Pamba te bato ya sembo bakovanda na mokili, mpe bato oyo bazangi pamela bakotikala kati na yango;
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
kasi bato mabe bakokufa na mokili mpe bakolongola bango kati na mokili ya bato ya songisongi.

< Miyambo 2 >