< Miyambo 2 >

1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
Fili mi, si susceperis sermones meos, et mandata mea absconderis penes te,
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
ut audiat sapientiam auris tua: inclina cor tuum ad cognoscendam prudentiam.
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
Si enim sapientiam invocaveris, et inclinaveris cor tuum prudentiae:
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
si quaesieris eam quasi pecuniam, et sicut thesauros effoderis illam:
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
tunc intelliges timorem Domini, et scientiam Dei invenies:
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
quia Dominus dat sapientiam: et ex ore eius prudentia, et scientia.
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
Custodiet rectorum salutem, et proteget gradientes simpliciter,
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
servans semitas iustitiae, et vias sanctorum custodiens.
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
Tunc intelliges iustitiam, et iudicium, et aequitatem, et omnem semitam bonam.
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
Si intraverit sapientia cor tuum, et scientia animae tuae placuerit:
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
consilium custodiet te, et prudentia servabit te,
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
ut eruaris a via mala, et ab homine, qui perversa loquitur:
13 amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
qui relinquunt iter rectum, et ambulant per vias tenebrosas:
14 amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
qui laetantur cum malefecerint, et exultant in rebus pessimis:
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
quorum viae perversae sunt, et infames gressus eorum.
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
Ut eruaris a muliere aliena, et ab extranea, quae mollit sermones suos,
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
et relinquit ducem pubertatis suae,
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
et pacti Dei sui oblita est. inclinata est enim ad mortem domus eius, et ad inferos semitae ipsius. (questioned)
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
omnes, qui ingrediuntur ad eam, non revertentur, nec apprehendent semitas vitae.
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
Ut ambules in via bona: et calles iustorum custodias.
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
Qui enim recti sunt, habitabunt in terra, et simplices permanebunt in ea.
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
Impii vero de terra perdentur: et qui inique agunt, auferentur ex ea.

< Miyambo 2 >