< Miyambo 2 >

1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
내 아들아 네가 만일 나의 말을 받으며 나의 계명을 네게 간직하며
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
네 귀를 지혜에 기울이며 네 마음을 명철에 두며
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
지식을 불러 구하며 명철을 얻으려고 소리를 높이며
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
은을 구하는 것 같이 그것을 구하며 감추인 보배를 찾는 것 같이 그것을 찾으면
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
여호와 경외하기를 깨달으며 하나님을 알게 되리니
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
대저 여호와는 지혜를 주시며 지식과 명철을 그 입에서 내심이며
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
그는 정직한 자를 위하여 완전한 지혜를 예비하시며 행실이 온전한 자에게 방패가 되시나니
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
대저 그는 공평의 길을 보호하시며 그 성도들의 길을 보전하려 하심이니라
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
그런즉 네가 공의와 공평과 정직 곧 모든 선한 길을 깨달을 것이라
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
곧 지혜가 네 마음에 들어가며 지식이 네 영혼에 즐겁게 될 것이요
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
근신이 너를 지키며 명철이 너를 보호하여
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
악한 자의 길과 패역을 말하는 자에게서 건져내리라
13 amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
이 무리는 정직한 길을 떠나 어두운 길로 행하며
14 amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
행악하기를 기뻐하며 악인의 패역을 즐거워하나니
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
그 길은 구부러지고 그 행위는 패역하리라
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
지혜가 또 너를 음녀에게서, 말로 호리는 이방 계집에게서 구원하리니
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
그는 소시의 짝을 버리며 그 하나님의 언약을 잊어버린자라
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
그 집은 사망으로, 그 길은 음부로 기울어졌나니
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
누구든지 그에게로 가는 자는 돌아오지 못하며 또 생명길을 얻지 못하느니라
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
지혜가 너로 선한 자의 길로 행하게 하며 또 의인의 길을 지키게 하리니
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
대저 정직한 자는 땅에 거하며 완전한 자는 땅에 남아 있으리라
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
그러나 악인은 땅에서 끊어지겠고 궤휼한 자는 땅에서 뽑히리라

< Miyambo 2 >