< Miyambo 2 >

1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
Mein Kind, so du willst meine Rede annehmen und meine Gebote bei dir behalten,
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
daß dein Ohr auf Weisheit achthat und du dein Herz mit Fleiß dazu neigest;
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
ja, so du mit Fleiß darnach rufest und darum betest;
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
so du sie suchest wie Silber und nach ihr froschest wie nach Schätzen:
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
alsdann wirst du die Furcht des HERRN verstehen und Gottes Erkenntnis finden.
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
Denn der HERR gibt Weisheit, und aus seinem Munde kommt Erkenntnis und Verstand.
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
Er läßt's den Aufrichtigen gelingen und beschirmt die Frommen
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
und behütet die, so recht tun, und bewahrt den Weg seiner Heiligen.
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
Alsdann wirst du verstehen Gerechtigkeit und Recht und Frömmigkeit und allen guten Weg.
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
Denn Weisheit wird in dein Herz eingehen, daß du gerne lernst;
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
guter Rat wird dich bewahren, und Verstand wird dich behüten,
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
daß du nicht geratest auf den Weg der Bösen noch unter die verkehrten Schwätzer,
13 amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
die da verlassen die rechte Bahn und gehen finstere Wege,
14 amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
die sich freuen, Böses zu tun, und sind fröhlich in ihrem bösen, verkehrten Wesen,
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
welche ihren Weg verkehren und folgen ihrem Abwege;
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
daß du nicht geratest an eines andern Weib, an eine Fremde, die glatte Worte gibt
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
und verläßt den Freund ihrer Jugend und vergißt den Bund ihres Gottes
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
(denn ihr Haus neigt sich zum Tod und ihre Gänge zu den Verlorenen;
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
alle, die zu ihr eingehen, kommen nicht wieder und ergreifen den Weg des Lebens nicht);
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
auf daß du wandelst auf gutem Wege und bleibst auf der rechten Bahn.
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
Denn die Gerechten werden im Lande wohnen, und die Frommen werden darin bleiben;
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
aber die Gottlosen werden aus dem Lande ausgerottet, und die Verächter werden daraus vertilgt.

< Miyambo 2 >