< Miyambo 2 >

1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
Mon fils, si tu reçois mes paroles, Et si tu gardes avec toi mes préceptes,
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
Si tu rends ton oreille attentive à la sagesse, Et si tu inclines ton cœur à l’intelligence;
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
Oui, si tu appelles la sagesse, Et si tu élèves ta voix vers l’intelligence,
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
Si tu la cherches comme l’argent, Si tu la poursuis comme un trésor,
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
Alors tu comprendras la crainte de l’Éternel, Et tu trouveras la connaissance de Dieu.
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
Car l’Éternel donne la sagesse; De sa bouche sortent la connaissance et l’intelligence;
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
Il tient en réserve le salut pour les hommes droits, Un bouclier pour ceux qui marchent dans l’intégrité,
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
En protégeant les sentiers de la justice Et en gardant la voie de ses fidèles.
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
Alors tu comprendras la justice, l’équité, La droiture, toutes les routes qui mènent au bien.
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
Car la sagesse viendra dans ton cœur, Et la connaissance fera les délices de ton âme;
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
La réflexion veillera sur toi, L’intelligence te gardera,
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
Pour te délivrer de la voie du mal, De l’homme qui tient des discours pervers,
13 amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
De ceux qui abandonnent les sentiers de la droiture Afin de marcher dans des chemins ténébreux,
14 amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
Qui trouvent de la jouissance à faire le mal, Qui mettent leur plaisir dans la perversité,
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
Qui suivent des sentiers détournés, Et qui prennent des routes tortueuses;
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
Pour te délivrer de la femme étrangère, De l’étrangère qui emploie des paroles doucereuses,
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
Qui abandonne l’ami de sa jeunesse, Et qui oublie l’alliance de son Dieu;
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
Car sa maison penche vers la mort, Et sa route mène chez les morts:
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
Aucun de ceux qui vont à elle ne revient, Et ne retrouve les sentiers de la vie.
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
Tu marcheras ainsi dans la voie des gens de bien, Tu garderas les sentiers des justes.
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
Car les hommes droits habiteront le pays, Les hommes intègres y resteront;
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
Mais les méchants seront retranchés du pays, Les infidèles en seront arrachés.

< Miyambo 2 >