< Miyambo 2 >

1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
O son my if you will receive words my and commandments my you will treasure with you.
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
To make attend to wisdom ear your you will incline heart your to understanding.
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
That except to discernment you will call to understanding you will give voice your.
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
If you will seek it like silver and like treasures you will search for it.
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
Then you will discern [the] fear of Yahweh and [the] knowledge of God you will find.
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
For Yahweh he gives wisdom from mouth his knowledge and understanding.
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
(He stores up *Q(K)*) for upright [people] success a shield to [those who] walk of integrity.
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
To guard [the] paths of justice and [the] way of (faithful [people] his *Q(K)*) he will preserve.
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
Then you will understand righteousness and justice and uprightness every course of good.
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
For it will come wisdom in heart your and knowledge to self your it will be pleasant.
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
Discretion it will watch over you understanding it will preserve you.
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
To deliver you from a way evil from anyone [who] speaks perverse things.
13 amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
Those [who] leave paths of uprightness to walk in [the] ways of darkness.
14 amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
The [ones] joyful to do evil they exult in perverse things of evil.
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
Who paths their [are] twisted and [who are] crooked in tracks their.
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
To deliver you from a woman strange from a foreign [woman] [who] words her she makes smooth.
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
Who leaves [the] close friend of youth her and [the] covenant of God her she forgets.
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
For she sank down to death house her and to [the] shades tracks her.
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
All [those who] go to her not they return! and not they reach [the] paths of life.
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
So that you may walk in [the] way of good [people] and [the] paths of righteous [people] you will keep.
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
For upright [people] (they will dwell *L(bah)*) [the] land and blameless [people] they will remain in it.
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
And wicked [people] from [the] land they will be cut off and treacherous [people] they will be torn away from it.

< Miyambo 2 >