< Miyambo 2 >

1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
My son, if thou wilt receive my words, and wilt hide my commandments with thee,
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
That thy ear may hearken to wisdom: Incline thy heart to know prudence:
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
For if thou shalt call for wisdom, and incline thy heart to prudence:
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
If thou shalt seek her as money, and shalt dig for her as for a treasure:
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
Then shalt thou understand the fear of the Lord, and shalt find the knowledge of God.
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
Because the Lord giveth wisdom: and out of his mouth cometh prudence and knowledge.
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
He will keep the salvation of the righteous, and protect them that walk in simplicity.
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
Keeping the paths of justice, and guarding the ways of saints.
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
Then shalt thou understand justice, and judgment, and equity, and every good path.
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
If wisdom shall enter into thy heart, and knowledge please thy soul:
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
Counsel shall keep thee, and prudence shall preserve thee,
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
That thou mayst be delivered from the evil way, and from the man that speaketh perverse things:
13 amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
Who leave the right way, and walk by dark ways:
14 amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
Who are glad when they have done evil, and rejoice in most wicked things:
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
Whose ways are perverse, and their steps infamous.
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
That thou mayst be delivered from the strange women, and from the stranger, who softeneth her words:
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
And forsaketh the guide of her youth,
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
And hath forgotten the covenant of her God: for her house inclineth unto death, and her paths to hell. (questioned)
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
None that go in unto her shall return again, neither shall they take hold of the paths of life,
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
That thou mayst walk in a good way: and mayst keep the paths of the just.
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
For they that are upright shall dwell in the earth, and the simple shall continue in it.
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
But the wicked shall be destroyed from the earth: and they that do unjustly shall be taken away from it.

< Miyambo 2 >