< Miyambo 2 >

1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
My son, if thou will receive my words, and lay up my commandments with thee,
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
so as to incline thine ear to wisdom, and apply thy heart to understanding,
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
yea, if thou cry after discernment, and lift up thy voice for understanding,
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
if thou seek her as silver, and search for her as for hidden treasures,
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
then thou shall understand the fear of Jehovah, and find the knowledge of God.
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
For Jehovah gives wisdom. Out of his mouth is knowledge and understanding.
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
He lays up sound wisdom for the upright, a shield to those who walk in integrity,
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
that he may guard the paths of justice, and preserve the way of his sanctified.
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
Then thou shall understand righteousness and justice and equity, yea, every good path.
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
For wisdom shall enter into thy heart, and knowledge shall be pleasant to thy soul,
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
discretion shall watch over thee, understanding shall keep thee,
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
to deliver thee from the way of evil, from the men who speak perverse things,
13 amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
who forsake the paths of uprightness to walk in the ways of darkness,
14 amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
who rejoice to do evil, and delight in the perverseness of evil,
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
who are crooked in their ways, and wayward in their paths,
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
to deliver thee from the interloping woman, even from the stranger who flatters with her words,
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
who forsakes the companion of her youth, and forgets the covenant of her God
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
(for her house inclines to death, and her paths to the dead;
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
none who go to her return again, nor do they attain to the paths of life),
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
that thou may walk in the way of good men, and keep the paths of the righteous.
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
For the upright shall dwell in the land, and the perfect shall remain in it.
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
But the wicked shall be cut off from the land, and the treacherous shall be rooted out of it.

< Miyambo 2 >