< Miyambo 2 >
1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
Wuoda, ka iyie rwako wechena kendo kano chikena e chunyi;
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
ka ichiko iti ni weche mag rieko kendo kiketo chunyi mondo iwinj tiend weche,
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
to ka imanyo ngʼeyo malingʼ-lingʼ, kendo ikwayo ngʼeyo tiend wach,
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
to ka idware ka fedha kendo imanye ka mwandu mopandi,
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
eka iniwinj malongʼo tiend luoro Jehova Nyasaye, kendo iniyud rieko mar ngʼeyo Nyasaye.
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
Jehova Nyasaye chiwo rieko kendo ngʼeyo gi winjo aa e dhoge.
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
Oiko loch ni joma kare, en okumba ni jogo ma wuodhgi ler,
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
nimar en okumba mar joma kare kendo orito yor joge ma jo-adiera.
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
Ka iwinjo wachna, eka iningʼe gima kare, kendo mowinjore ma gin yore duto mabeyo.
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
Nimar rieko nodonj e chunyi, kendo ngʼeyo nomi ngimani bedo mamor.
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
Rieko mar pogo tiend wach noriti, kendo winjo tiend wach nobedni okumba.
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
Rieko noresi kuom yore mag joma mono, kuom jogo mawacho weche mochido,
13 amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
jogo moweyo yore moriere mag bidhruok, mondo giwuothi e yore mag mudho,
14 amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
joma mor kuom timo maricho kendo giil e duwruok mar richo,
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
jogo ma yoregi ogajore ogajore kendo gin jowuond e yoregi.
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
Bende enoresi kuom dhako ma jachode, kuom dhako mabayo gi wechege maywayo ji,
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
moseweyo chwore mane okende konyako, kendo oketho singruok mane otimo e nyim Nyasaye.
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
Nikech ode tero ji e tho to yorene tero ji e piny joma otho.
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
Onge ngʼato madhi ire maduogo kata yudo yor ngima.
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
Kuom mano, iniluw yore joma beyo kendo irit yore joma kare.
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
Nimar joma kare ema nodag e piny kendo jogo maonge bura ema nosiki e piny;
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
to joma timbegi mono nogol oko e piny kendo jogo ma ok jo-adiera ok nobedie ngangʼ.