< Miyambo 2 >

1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
Min Søn, når du tager imod mine ord og gemmer mine Pålæg hos dig,
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
idet du låner Visdom Øre og bøjer dit Hjerte til Indsigt,
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
ja, kalder du på Forstanden og løfter din Røst efter Indsigt,
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
søger du den som Sølv og leder den op som Skatte,
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
da nemmer du HERRENs Frygt og vinder dig Kundskab om Gud.
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
Thi HERREN, han giver Visdom, fra hans Mund kommer Kundskab og Indsigt.
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
Til retsindige gemmer han Lykke, han er Skjold for alle med lydefri Vandel,
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
idet han værner Rettens Stier og vogter sine frommes Vej.
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
Da nemmer du Retfærd, Ret og Retsind, hvert et Spor, som er godt.
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
Thi Visdom kommer i dit Hjerte, og Kundskab er liflig for din Sjæl;
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
Kløgt skal våge over dig, Indsigt være din Vogter -
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
idet den frier dig fra den ondes Vej, fra Folk, hvis Ord kun er vrange, -
13 amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
som går fra de lige Stier for at vandre på Mørkets Veje.
14 amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
som glæder sig ved at gøre ondt og jubler over vrangt og ondt,
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
de, som går krogede Stier og følger bugtede Spor -
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
idet den frier dig fra Andenmands Hustru, fra fremmed Kvinde med sleske Ord,
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
der sviger sin Ungdoms Ven og glemmer sin Guds Pagt;
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
thi en Grav til Døden er hendes Hus, til Skyggerne fører hendes Spor;
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
tilbage vender ingen, som går ind til hende, de når ej Livets Stier
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
at du må vandre de godes Vej og holde dig til de retfærdiges Stier;
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
thi retsindige skal bo i Landet, lydefri levnes deri,
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
men gudløse ryddes af Landet, troløse rykkes derfra.

< Miyambo 2 >