< Miyambo 2 >

1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
Ka capa, ka lawk hah ngâi nateh, kaie kâpoelawknaw e hah na lungthung vah na pâkuem pawiteh,
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
Lungangnae koe lah na hnâpakeng nateh, na thai panuek nahanelah na lungthin na poe pawiteh,
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
Kapek thai nahanelah na kaw teh, thaipanueknae tawn hanelah na hram pawiteh,
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
ngun patetlah na tawng teh, hro e hno patetlah na tawng pawiteh,
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
BAWIPA takinae na panue vaiteh, Cathut panuenae hah na hmu han.
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
Bangkongtetpawiteh, BAWIPA ni lungangnae a poe teh, a pahni hoi panuenae hoi thaipanueknae hah ouk a tâco sak.
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
Tamikalannaw hanelah lungangnae katang hah a pâkhueng pouh teh, kalan lah kacetnaw hanelah bahling lah ao.
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
Kângingnae lam hah a ring teh, a tamikathoungnaw e lamthung hah a ngue pouh.
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
Hottelahoi, kângingnae hoi lannae na thaipanuek vaiteh, ngaima tawnhoehnae hoi kahawi e lamthung hai na panue han.
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
Na lungthin dawk lungangnae a kâen toteh, panuenae teh, na hringnae kanawm sakkung lah ao han.
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
Poukpanueknae ni na ngue vaiteh, thaipanueknae ni na ring han.
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
Tamikathoutnaw e lamthung dawk hoi na rungngang han. Lawk longkawi lah ka dei e,
13 amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
Lannae lamthung ka pahnawt niteh, hmonae lamthung dawn hanelah ka cet e,
14 amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
thoenae saknae dawk lungkahawi e, tamikathout lanhoehnae dawk a lungkahawi e,
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
Lam longkawi ka dawn niteh, a lamthung dawk yuemkamcu hoeh e,
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
Kahlong lae napui hoi pasawtpanep lawk ka hno e,
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
A naw nah hui ka cettakhai niteh, a Cathut lawkkam kapahnimnaw koehoi nang hah na rungngang han.
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
Bangkongtetpawiteh, ahnie im ni duenae koe lah a hrawi teh, ahnie lam ni tamikadoutnaw koelah a pâtam.
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
Ahni koe kacetnaw teh ban boihoeh toe. Hringnae lam hah dawn boi awh hoeh toe.
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
Nang teh tamikahawinaw e lamthung na dawn vaiteh, lannae lamthung pou na dawn thai nahane doeh.
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
Bangkongtetpawiteh, tamikalan teh ram dawk kho a sak vaiteh, tami kakuep teh hawvah pou ao han.
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
Hatei, tamikathout teh talai van hoi takhoe lah awm vaiteh, yuemkamcu hoeh naw hah phawk lah ao awh han.

< Miyambo 2 >