< Miyambo 19 >

1 Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.
Mejor es el pobre que camina en su simplicidad, que el de perversos labios, e insensato.
2 Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.
El alma sin ciencia no es buena; y el presuroso de pies, peca.
3 Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova.
La insensatez del hombre tuerce su camino; y contra Jehová se aira su corazón.
4 Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.
Las riquezas allegan muchos amigos: mas el pobre, de su amigo es apartado.
5 Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.
El testigo falso no será sin castigo; y el que habla mentiras, no escapará.
6 Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.
Muchos rogarán al príncipe: mas cada uno es amigo del hombre que da.
7 Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.
Todos los hermanos del pobre le aborrecen, ¿cuánto más sus amigos se alejarán de él? buscará la palabra, y no la hallará.
8 Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.
El que posee entendimiento, ama su alma: guarda la inteligencia, para hallar el bien.
9 Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.
El testigo falso no será sin castigo; y el que habla mentiras, perecerá.
10 Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!
No conviene al insensato la delicia, ¿cuánto menos al siervo ser señor de los príncipes?
11 Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.
El entendimiento del hombre detiene su furor; y su honra es disimular la prevaricación.
12 Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.
Como el bramido del cachorro del león es la ira del rey; y como el rocío sobre la yerba su benevolencia.
13 Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.
Dolor es para su padre el hijo insensato; y gotera continua las contiendas de la mujer.
14 Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.
La casa y las riquezas herencia son de los padres: mas de Jehová la mujer prudente.
15 Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.
La pereza hace caer sueño; y el alma negligente hambreará.
16 Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.
El que guarda el mandamiento, guarda su alma: mas el que menospreciare sus caminos, morirá.
17 Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.
A Jehová empresta el que da al pobre; y él le dará su paga.
18 Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake.
Castiga a tu hijo entre tanto que hay esperanza: mas para matarle no alces tu voluntad.
19 Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.
El de grande ira, llevará la pena; porque aun si le librares, todavía tornarás.
20 Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru.
Escucha el consejo, y recibe la enseñanza, para que seas sabio en tu vejez.
21 Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.
Muchos pensamientos están en el corazón del hombre: mas el consejo de Jehová permanecerá.
22 Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.
Contentamiento es a los hombres hacer misericordia; y el pobre es mejor que el mentiroso.
23 Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.
El temor de Jehová es para vida; y permanecerá harto: no será visitado de mal.
24 Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.
El perezoso esconde su mano en el seno: aun a su boca no la llevará.
25 Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.
Hiere al burlador, y el simple se hará avisado; y corrigiendo al entendido, entenderá ciencia.
26 Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.
El que roba a su padre, y ahuyenta a su madre, hijo es avergonzador, y deshonrador.
27 Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.
Cesa, hijo mío, de oír el enseñamiento, que te haga desviar de las razones de sabiduría.
28 Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.
El testigo perverso se burlará del juicio; y la boca de los impíos encubrirá la iniquidad.
29 Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.
Aparejados están juicios para los burladores; y azotes para los cuerpos de los insensatos.

< Miyambo 19 >