< Miyambo 19 >

1 Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.
Май мулт прецуеште сэракул каре умблэ ын неприхэниря луй декыт ун богат ку бузе стрикате ши небун.
2 Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.
Липса де штиинцэ есте о пагубэ пентру чинева ши чине аляргэ негьобеште ынаинте о нимереште рэу.
3 Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova.
Небуния омулуй ый сучеште каля ши апой кыртеште ымпотрива Домнулуй ку инима луй.
4 Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.
Богэция адуче ун маре нумэр де приетень, дар сэракул есте пэрэсит де приетенул луй.
5 Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.
Марторул минчинос ну рэмыне непедепсит ши чел че спуне минчунь ну ва скэпа.
6 Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.
Омул дарник аре мулць лингушиторь ши тоць сунт приетень ку чел че дэ дарурь.
7 Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.
Тоць фраций сэракулуй ыл урэск; ку кыт май мулт се депэртязэ приетений луй де ел! Ел се ындряптэ спре ей ку ворбе ругэтоаре, дар ей се фак невэзуць.
8 Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.
Чине капэтэ ынцелепчуне ышь юбеште суфлетул; чине пэстрязэ причеперя гэсеште феричиря.
9 Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.
Марторул минчинос ну рэмыне непедепсит ши чел че спуне минчунь ва пери.
10 Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!
Унуй небун ну-й шаде бине сэ трэяскэ ын десфэтэрь, ку атыт май пуцин унуй роб, сэ стэпыняскэ песте воевозь.
11 Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.
Ынцелепчуня фаче пе ом рэбдэтор ши есте о чинсте пентру ел сэ уйте грешелиле.
12 Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.
Мыния ымпэратулуй есте ка рэкнетул унуй леу ши бунэвоинца луй есте ка роуа пе ярбэ.
13 Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.
Ун фиу небун есте о ненорочире пентру татэл сэу, ши о невастэ гылчевитоаре есте ка о стряшинэ де пе каре пикурэ ынтруна.
14 Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.
Каса ши аверя ле моштеним де ла пэринць, дар о невастэ причепутэ есте ун дар де ла Домнул.
15 Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.
Леня те куфундэ ынтр-ун сомн адынк ши суфлетул молатик суферэ де фоаме.
16 Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.
Чине пэзеште порунка ышь пэзеште суфлетул; чине ну вегязэ асупра кэий сале ва мури.
17 Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.
Чине аре милэ де сэрак ымпрумутэ пе Домнул, ши Ел ый ва рэсплэти бинефачеря.
18 Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake.
Педепсеште-ць фиул, кэч тот май есте нэдежде, дар ну дори сэ-л оморь!
19 Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.
Чел пе каре-л апукэ мыния требуе сэ-шь я педяпса; кэч, дакэ-л скоць дин еа, ва требуи сэ май фачь о датэ лукрул ачеста.
20 Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru.
Аскултэ сфатуриле ши примеште ынвэцэтура, ка сэ фий ынцелепт пе виитор!
21 Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.
Омул фаче мулте планурь ын инима луй, дар хотэрыря Домнулуй, ачея се ымплинеште.
22 Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.
Чея че фаче фармекул унуй ом есте бунэтатя луй; ши май мулт прецуеште ун сэрак декыт ун минчинос.
23 Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.
Фрика де Домнул дуче ла вяцэ, ши чел че о аре петрече ноаптя сэтул, фэрэ сэ фие черчетат де ненорочире.
24 Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.
Ленешул ышь вырэ мына ын стракинэ ши н-о дуче ынапой ла гурэ.
25 Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.
Ловеште пе батжокоритор ши простул се ва фаче ынцелепт; мустрэ пе омул причепут ши ва ынцелеӂе штиинца!
26 Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.
Чине жефуеште пе татэл сэу ши изгонеште пе мама са есте ун фиу каре адуче рушине ши окарэ.
27 Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.
Ынчетязэ, фиуле, сэ май аскулць ынвэцэтура, дакэ еа те депэртязэ де ынвэцэтуриле ынцелепте.
28 Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.
Ун мартор стрикат ышь бате жок де дрептате ши гура челор рэй ынгите нелеӂюиря.
29 Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.
Педепселе сунт прегэтите пентру батжокориторь ши ловитуриле, пентру спинэриле небунилор.

< Miyambo 19 >