< Miyambo 19 >

1 Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.
Bedre er en fattig som vandrer i ustraffelighet, enn en mann med falske leber, som tillike er en dåre.
2 Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.
Også den som ikke bruker omtanke, går det ille, og den som er for snar på foten, treder feil.
3 Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova.
Menneskets egen dårskap ødelegger hans vei, men i sitt hjerte vredes han på Herren.
4 Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.
Rikdom skaper mange venner, den fattige blir skilt fra sin venn.
5 Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.
Et falskt vidne skal ikke bli ustraffet, og den som taler løgn, skal ikke komme unda.
6 Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.
Mange smigrer for den gavmilde, og enhver er venn med den som er rundhåndet.
7 Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.
Den fattiges frender hater ham alle; enda mere holder hans venner sig borte fra ham. Han jager efter ord som ikke er å finne.
8 Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.
Den som vinner forstand, elsker sitt liv; den som holder fast ved visdom, finner lykke.
9 Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.
Et falskt vidne skal ikke bli ustraffet, og den som taler løgn, skal omkomme.
10 Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!
Vellevnet høver ikke for en dåre, enda mindre høver det for en træl å herske over fyrster.
11 Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.
Et menneskes klokskap gjør ham langmodig, og det er hans ære at han overser krenkelser.
12 Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.
En konges vrede er som løvens brøl, men hans yndest som dugg på urter.
13 Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.
En uforstandig sønn er bare til ulykke for sin far, og en kvinnes tretter er et stadig takdrypp.
14 Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.
Hus og gods er en arv fra foreldre, men en forstandig kvinne er en gave fra Herren.
15 Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.
Dovenskap senker i dyp søvn, og den late skal hungre.
16 Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.
Den som holder budet, holder sig selv i live; den som ikke akter på sin ferd, skal miste sitt liv.
17 Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.
Den som forbarmer sig over den fattige, låner til Herren, og Herren skal gjengjelde ham hans velgjerning.
18 Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake.
Tukt din sønn, for det er ennu håp; men la dig ikke drive til å drepe ham!
19 Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.
Den hvis vrede er stor, bør bøte; for dersom du hjelper ham, får du gjøre det atter og atter.
20 Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru.
Hør på råd og ta imot tukt, så du kan bli vis til slutt!
21 Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.
Det er mange tanker i en manns hjerte, men Herrens råd skal få fremgang.
22 Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.
Et menneskes miskunnhet er hans glede, og en fattig er lykkeligere enn en stormann som lyver.
23 Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.
Herrens frykt fører til liv, og mett får en gå til hvile uten å bli hjemsøkt med ulykke.
24 Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.
Den late stikker sin hånd i fatet, men fører den ikke engang tilbake til sin munn.
25 Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.
Slå spotteren, så vil den uforstandige bli klok; vis den forstandige til rette, så vil han komme til innsikt og kunnskap.
26 Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.
Den som bruker vold mot sin far og jager sin mor bort, er en dårlig, en skamløs sønn.
27 Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.
Hold op, min sønn, med å høre på formaning, når du allikevel bare forviller dig bort fra kunnskaps ord!
28 Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.
Et ugudelig vidne spotter det som rett er, og de gudløses munn sluker urett.
29 Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.
Straffedommer er fastsatt for spotterne og pryl for dårers rygg.

< Miyambo 19 >