< Miyambo 19 >
1 Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.
Jobb a szegény, a ki gáncstalanságában jár, mint az álnok ajkú, a ki balga.
2 Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.
Hogy lélek tudás nélkül van, az sem jó, és a ki lábaival hamarkodik, vétkezik.
3 Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova.
Az ember oktalansága elferdíti útját, és az Örökkévaló ellen háborog szíve.
4 Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.
A vagyon hozzászerez sok barátot, de a szegénynek a társa is elválik.
5 Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.
Hazug tanú nem marad büntetlenül, és a ki hazugságokat terjeszt, nem menekül meg.
6 Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.
Sokan hízelegnek a bőkezűnek, és mindenki barátja az adakozó embernek.
7 Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.
A szegénynek minden testvérei gyűlölik őt, mennyivel inkább távoznak tőle társai. Ki szóbeszédet hajhász, az övé az.
8 Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.
A ki szívet szerez, szereti lelkét, a ki megőrzi az értelmet, jót fog találni.
9 Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.
Hazug tanú nem marad büntetlenül, s a ki hazugságokat terjeszt, elvész.
10 Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!
Nem illik a balgához a gyönyörködés, hát még a szolgához uralkodni urakon!
11 Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.
Az embernek esze hosszantűrővé teszi, és díszessége: elnézni a büntettet.
12 Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.
Mint a fiatal oroszlán ordítása, olyan a király haragja, s mint harmat a fűre az ő kegye.
13 Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.
Veszedelmére van atyjának a balga fiú, és csepegő eresz az asszony czivódása.
14 Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.
Ház és vagyon ősök öröke, de az Örökkévalótól van az eszes asszony.
15 Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.
Restség mély álomba ejt, és a renyhének lelke éhezik.
16 Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.
A ki megőrzi a parancsolatot, megőrzi lelkét, a ki megveti utjait, meg fog halni.
17 Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.
Az Örökkévalónak ad kölcsön, ki könyörül a szegényen, és tettét megfizeti néki.
18 Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake.
Fenyítsd fiadat, mert van remény, de megölésére ne vidd lelkedet.
19 Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.
A nagy indulatú viseli a bírságot, mert ha megmentenéd, még növelnéd.
20 Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru.
Halljad a tanácsot és fogadd el az oktatást, azért hogy bölcs légy a végeden.
21 Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.
Sok a gondolat a férfi szívében, de az Örökkévaló tanácsa – az áll fönn.
22 Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.
Az ember kívánsága az ő szeretete, és jobb a szegény a hazugság emberénél.
23 Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.
Az Istenfélelem életre visz, s jóllakottan hál meg, nem ér hozzá baj.
24 Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.
Bedugta kezét a rest a tálba, még a szájához sem viszi vissza.
25 Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.
A csúfolót ütöd és az együgyű lesz okossá; s ha feddik az értelmest, megérti a tudást.
26 Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.
Atyját pusztítja, anyját megfutamítja szégyenletes és gyalázatos fi.
27 Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.
Hallgatva oktatásra, szűnj meg, fiam, eltévelyegni a tudás szavaitól!
28 Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.
Alávaló tanú megcsúfolja a jogot, és a gonoszok szája elnyeli a jogtalanságot.
29 Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.
Készen vannak a csúfolóknak a büntetések és ütlegek a balgák hátának.