< Miyambo 19 >
1 Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.
Better is the poor that walketh in his integrity than he that perverse in his lips and is a fool.
2 Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.
Also, that the soul be without knowledge is not good; and he that hasteth with his feet sinneth.
3 Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova.
The foolishness of man subverteth his way; and his heart fretteth against the LORD.
4 Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.
Wealth addeth many friends: but the poor is separated from his friend.
5 Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.
A false witness shall not be unpunished; and he that uttereth lies shall not escape.
6 Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.
Many will entreat the favour of the liberal man: and every man is a friend to him that giveth gifts.
7 Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.
All the brethren of the poor do hate him: how much more do his friends go far from him! he pursueth [them with] words, [but] they are gone.
8 Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.
He that getteth wisdom loveth his own soul: he that keepeth understanding shall find good.
9 Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.
A false witness shall not be unpunished; and he that uttereth lies shall perish.
10 Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!
Delicate living is not seemly for a fool; much less for a servant to have rule over princes.
11 Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.
The discretion of a man maketh him slow to anger; and it is his glory to pass over a transgression.
12 Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.
The king’s wrath is as the roaring of a lion; but his favour is as dew upon the grass.
13 Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.
A foolish son is the calamity of his father: and the contentions of a wife are a continual dropping.
14 Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.
House and riches are an inheritance from fathers: but a prudent wife is from the LORD.
15 Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.
Slothfulness casteth into a deep sleep; and the idle soul shall suffer hunger.
16 Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.
He that keepeth the commandment keepeth his soul: [but] he that is careless of his ways shall die.
17 Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.
He that hath pity upon the poor lendeth unto the LORD, and his good deed will he pay him again.
18 Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake.
Chasten thy son, seeing there is hope; and set not thy heart on his destruction.
19 Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.
A man of great wrath shall bear the penalty: for if thou deliver [him], thou must do it yet again.
20 Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru.
Hear counsel, and receive instruction, that thou mayest be wise in thy latter end.
21 Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.
There are many devices in a man’s heart; but the counsel of the LORD, that shall stand.
22 Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.
The desire of a man is [the measure of] his kindness: and a poor man is better than a liar.
23 Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.
The fear of the LORD [tendeth] to life: and he [that hath it] shall abide satisfied; he shall not be visited with evil.
24 Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.
The sluggard burieth his hand in the dish, and will not so much as bring it to his mouth again.
25 Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.
smite a scorner, and the simple will learn prudence: and reprove one that hath understanding, [and] he will understand knowledge.
26 Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.
He that spoileth his father, and chaseth away his mother, is a son that causeth shame and bringeth reproach.
27 Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.
Cease, my son, to hear instruction [only] to err from the words of knowledge.
28 Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.
A worthless witness mocketh at judgment: and the mouth of the wicked swalloweth iniquity.
29 Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.
Judgments are prepared for scorners, and stripes for the back of fools.