< Miyambo 18 >

1 Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
Conforme al deseo busca el apartado: en toda doctrina se envolverá.
2 Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
No toma placer el insensato en la inteligencia: mas en lo que se descubre su corazón.
3 Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
Cuando viene el impío, viene también el menosprecio; y con el deshonrador, la vergüenza.
4 Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
Aguas profundas son las palabras de la boca del hombre; y arroyo revertiente la fuente de la sabiduría.
5 Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
Tener respeto a la persona del impío, para hacer caer al justo de su derecho, no es bueno.
6 Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
Los labios del insensato vienen con pleito; y su boca a cuestiones llama.
7 Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
La boca del insensato es quebrantamiento para sí; y sus labios son lazos para su alma.
8 Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
Las palabras del chismoso parecen blandas: mas ellas descienden hasta lo íntimo del vientre.
9 Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
También el que es negligente en su obra, es hermano del dueño disipador.
10 Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
Torre fuerte es el nombre de Jehová: a él correrá el justo, y será levantado.
11 Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
Las riquezas del rico son la ciudad de su fortaleza; y como un muro alto, en su imaginación.
12 Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
Antes del quebrantamiento se eleva el corazón del hombre; y antes de la honra, el abatimiento.
13 Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
El que responde palabra antes de oír, insensatez le es, y vergüenza.
14 Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
El ánimo del hombre suportará su enfermedad: mas al ánimo angustiado, ¿quién le suportará?
15 Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
El corazón del entendido adquiere sabiduría; y el oído de los sabios busca la ciencia.
16 Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
El presente del hombre le ensancha el camino; y le lleva delante de los grandes.
17 Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
El justo es primero en su pleito; y su adversario viene, y búscale.
18 Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
La suerte pone fin a los pleitos; y desparte los fuertes.
19 Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
El hermano ofendido es más contumaz que una ciudad fuerte; y las contiendas de los hermanos son como cerrojos de alcázar.
20 Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
Del fruto de la boca del hombre se hartará su vientre: de la renta de sus labios se hartará.
21 Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
La muerte y la vida están en poder de la lengua; y el que la ama, comerá de sus frutos.
22 Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
El que halló mujer, halló el bien; y alcanzó la benevolencia de Jehová.
23 Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
El pobre habla ruegos; mas el rico responde durezas.
24 Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.
El hombre de amigos mantiénese en amistad; y a veces hay amigo más conjunto que el hermano.

< Miyambo 18 >