< Miyambo 18 >

1 Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
Човек самовољан тражи шта је њему мило и меша се у свашта.
2 Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
Безумнику није мио разум него да се јавља срце његово.
3 Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
Кад дође безбожник, дође и руг, и прекор са срамотом.
4 Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
Речи су из уста човечијих дубока вода, извор је мудрости поток који се разлива.
5 Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
Није добро гледати безбожнику ко је, да се учини криво правом на суду.
6 Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
Усне безумникове пристају у свађу, и уста његова дозивају бој.
7 Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
Безумнику су уста његова погибао, и усне његове пругло души његовој.
8 Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
Речи су опадачеве као избијених, али силазе унутра у трбух.
9 Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
И ко је немаран у послу свом брат је распикући.
10 Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
Тврда је кула име Господње. К Њему ће побећи праведник, и биће у високом заклону.
11 Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
Богатство је богатом јак град и као висок зид у његовој мисли.
12 Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
Пред пропаст подиже се срце човека, а пре славе иде смерност.
13 Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
Ко одговара пре него чује, томе је лудост и срамота.
14 Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
Дух човечији сноси бол свој; а дух оборен ко ће подигнути?
15 Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
Срце разумног човека добавља знање, и ухо мудрих тражи знање.
16 Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
Дар човеку шири место и води га пред властеље.
17 Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
Праведан се чини ко је први у својој распри, али кад дође ближњи његов, испитује се.
18 Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
Распре прекида жреб, и између силних расуђује.
19 Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
Увређен је брат као тврд град, и свађа је као преворница на двору.
20 Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
Сваком се трбух сити плодом уста његових, дохотком од усна својих сити се.
21 Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
Смрт је и живот у власти језику, и ко га милује, јешће плод његов.
22 Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
Ко је нашао жену, нашао је добро и добио љубав од Господа.
23 Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
Сиромах говори молећи, а богат одговара оштро.
24 Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.
Ко има пријатеља, ваља да поступа пријатељски, јер има пријатеља вернијих од брата.

< Miyambo 18 >