< Miyambo 18 >

1 Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
人と交わりをしない者は口実を捜し、すべてのよい考えに激しく反対する。
2 Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
愚かな者は悟ることを喜ばず、ただ自分の意見を言い表わすことを喜ぶ。
3 Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
悪しき者が来ると、卑しめもまた来る、不名誉が来ると、はずかしめも共にくる。
4 Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
人の口の言葉は深い水のようだ、知恵の泉は、わいて流れる川である。
5 Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
悪しき者をえこひいきすることは良くない、正しい者をさばいて、悪しき者とすることも良くない。
6 Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
愚かな者のくちびるは争いを起し、その口はむち打たれることを招く。
7 Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
愚かな者の口は自分の滅びとなり、そのくちびるは自分を捕えるわなとなる。
8 Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
人のよしあしをいう者の言葉はおいしい食物のようで、腹の奥にしみこむ。
9 Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
その仕事を怠る者は、滅ぼす者の兄弟である。
10 Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
主の名は堅固なやぐらのようだ、正しい者はその中に走りこんで救を得る。
11 Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
富める者の富はその堅き城である、それは高き城壁のように彼を守る。
12 Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
人の心の高ぶりは滅びにさきだち、謙遜は栄誉にさきだつ。
13 Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
事をよく聞かないで答える者は、愚かであって恥をこうむる。
14 Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
人の心は病苦をも忍ぶ、しかし心の痛むときは、だれがそれに耐えようか。
15 Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
さとき者の心は知識を得、知恵ある者の耳は知識を求める。
16 Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
人の贈り物は、その人のために道をひらき、また尊い人の前に彼を導く。
17 Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
先に訴え出る者は正しいように見える、しかしその訴えられた人が来て、それを調べて、事は明らかになる。
18 Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
くじは争いをとどめ、かつ強い争い相手の間を決定する。
19 Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
助けあう兄弟は堅固な城のようだ、しかし争いは、やぐらの貫の木のようだ。
20 Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
人は自分の言葉の結ぶ実によって、満ち足り、そのくちびるの産物によって自ら飽きる。
21 Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
死と生とは舌に支配される、これを愛する者はその実を食べる。
22 Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
妻を得る者は、良き物を得る、かつ主から恵みを与えられる。
23 Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
貧しい者は、あわれみを請い、富める者は、はげしい答をする。
24 Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.
世には友らしい見せかけの友がある、しかし兄弟よりもたのもしい友もある。

< Miyambo 18 >