< Miyambo 18 >

1 Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
Celui qui veut rompre avec son ami en cherche les occasions; mais il sera couvert d’opprobre en tout temps.
2 Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
L’insensé ne reçoit pas les paroles de la prudence, à moins que tu ne lui dises les choses qui se trouvent dans son cœur.
3 Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
L’impie, lorsqu’il est venu au fond des péchés, méprise; mais l’ignominie le suit ainsi que l’opprobre.
4 Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
C’est une eau profonde que les paroles qui sortent de la bouche de l’homme, et un torrent débordé que la source de la sagesse.
5 Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
Faire acception de la personne d’un impie n’est pas une bonne chose, pour que tu t’écartes de la vérité dans le jugement.
6 Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
Les lèvres de l’insensé se mêlent dans des rixes, et sa bouche provoque des querelles.
7 Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
La bouche de l’insensé est sa destruction; et ses lèvres sont la ruine de son âme.
8 Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
Les paroles d’un homme à double langue paraissent simples; et elles pénètrent jusqu’au fond des entrailles. La crainte abat le paresseux; mais les âmes des efféminés auront faim.
9 Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
Celui qui est mou et lâche dans son ouvrage est frère de celui qui détruit les ouvrages.
10 Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
C’est une tour très forte que le nom du Seigneur; le juste y court, et il sera exalté.
11 Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
Le bien du riche est sa ville forte, et comme une muraille solide qui l’environne.
12 Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
Avant qu’il soit brisé, le cœur de l’homme est exalté; et avant d’être élevé en gloire, il est humilié.
13 Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
Celui qui répond avant d’écouter se montre insensé et digne de confusion.
14 Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
L’esprit de l’homme soutient sa faiblesse; mais un esprit facile à se mettre en colère, qui pourra le soutenir?
15 Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
Le cœur prudent possédera la science; et l’oreille des sages cherche la doctrine.
16 Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
Le présent d’un homme élargit sa voie, et devant les princes lui fait faire place.
17 Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
Le juste est le premier accusateur de lui-même; vient son ami, et il l’examinera.
18 Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
Le sort apaise les différends; et entre les puissants mêmes, il sert d’arbitre.
19 Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
Un frère qui est aidé par son frère est comme une cité forte; et leurs jugements sont comme les verrous des portes des villes.
20 Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
Le ventre de l’homme sera rempli du fruit de sa bouche; et les produits de ses lèvres le rassasieront.
21 Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
La mort et la vie sont au pouvoir de la langue; ceux qui l’aiment mangeront ses fruits.
22 Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
Celui qui a trouvé une femme vertueuse a trouvé un bien; et il puisera la joie dans le Seigneur. Celui qui chasse une femme vertueuse rejette un bien; mais celui qui retient une adultère est insensé et impie.
23 Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
C’est avec des supplications que parlera le pauvre; mais le riche s’énoncera sévèrement.
24 Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.
L’homme aimable à la société sera plus ami qu’un frère.

< Miyambo 18 >