< Miyambo 18 >

1 Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
Celui qui se tient à l'écart ne cherche qu'à contenter sa passion, il s'irrite contre tout sage conseil.
2 Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
Ce n'est pas l'intelligence qui plaît à l'insensé, c'est la manifestation de ses pensées.
3 Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
Quand vient le méchant, vient aussi le mépris, et avec la honte vient l'opprobre.
4 Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
Les paroles de la bouche de l'homme sont des eaux profondes; la source de la sagesse est un torrent qui déborde.
5 Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
Il n'est pas bon d'avoir égard à la personne du méchant, pour faire tort au juste dans le jugement.
6 Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
Les lèvres de l'insensé se mêlent aux querelles et sa bouche provoque les outrages.
7 Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
La bouche de l'insensé cause sa ruine, et ses lèvres sont un piège pour son âme.
8 Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
Les paroles du rapporteur sont des morceaux friands, elles descendent jusqu'au fond des entrailles.
9 Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
Celui qui est lâche dans son travail est frère de celui qui va à la perdition.
10 Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
Le nom de Yahweh est une tour forte; le juste s'y réfugie et y est en sûreté.
11 Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
La fortune du riche est sa ville forte; dans sa pensée, c'est une muraille élevée.
12 Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
Avant la ruine, le cœur de l'homme s'élève, mais l'humilité précède la gloire.
13 Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
Celui qui répond avant d'avoir écouté, c'est pour lui folie et confusion.
14 Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
L'esprit de l'homme le soutient dans la maladie mais l'esprit abattu, qui le relèvera?
15 Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
Un cœur intelligent acquiert la science, et l'oreille des sages cherche la science.
16 Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
Le présent d'un homme lui élargit la voie, et l'introduit auprès des grands.
17 Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
Le premier qui expose sa cause paraît juste; vient la partie adverse, et on examine le différend.
18 Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
Le sort fait cesser les contestations, et décide entre les puissants.
19 Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
Un frère ennemi de son frère résiste plus qu'une ville forte, et leurs querelles sont comme les verrous d'un palais.
20 Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
C'est du fruit de la bouche de l'homme que se nourrit son corps, du produit de ses lèvres qu'il se rassasie.
21 Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
La mort et la vie sont au pouvoir de la langue; suivant son choix, on mangera ses fruits.
22 Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
Celui qui trouve une femme trouve le bonheur; c'est une faveur qu'il a reçue de Yahweh.
23 Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
Le pauvre parle en suppliant, et le riche répond durement.
24 Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.
L'homme aux nombreux amis les a pour sa perte, mais il tel ami plus attaché qu'un frère.

< Miyambo 18 >