< Miyambo 18 >

1 Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
He that separateth himself seeketh [his own] desire, and rageth against all sound wisdom.
2 Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
A fool hath no delight in understanding, but only that his heart may reveal itself.
3 Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
When the wicked cometh, there cometh also contempt, and with ignominy cometh reproach.
4 Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
The words of a man’s mouth are as deep waters; the wellspring of wisdom is as a flowing brook.
5 Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
To accept the person of the wicked is not good, [nor] to turn aside the righteous in judgment.
6 Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
A fool’s lips enter into contention, and his mouth calleth for stripes.
7 Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
A fool’s mouth is his destruction, and his lips are the snare of his soul.
8 Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
The words of a whisperer are as dainty, morsels, and they go down into the innermost parts of the belly.
9 Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
He also that is slack in his work is brother to him that is a destroyer.
10 Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
The name of the LORD is a strong tower: the righteous runneth into it, and is safe.
11 Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
The rich man’s wealth is his strong city, and as an high wall in his own imagination.
12 Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
Before destruction the heart of man is haughty, and before honour [goeth] humility.
13 Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
He that giveth answer before he heareth, it is folly and shame unto him.
14 Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
The spirit of a man will sustain his infirmity; but a broken spirit who can bear?
15 Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
The heart of the prudent getteth knowledge; and the ear of the wise seeketh knowledge.
16 Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
A man’s gift maketh room for him, and bringeth him before great men.
17 Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
He that pleadeth his cause first [seemeth] just; but his neighbour cometh and searcheth him out.
18 Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
The lot causeth contentions to cease, and parteth between the mighty.
19 Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
A brother offended [is harder to be won] than a strong city: and [such] contentions are like the bars of a castle.
20 Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
A man’s belly shall be filled with the fruit of his mouth; with the increase of his lips shall he be satisfied.
21 Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
Death and life are in the power of the tongue; and they that love it shall eat the fruit thereof.
22 Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
Whoso findeth a wife findeth a good thing, and obtaineth favour of the LORD.
23 Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
The poor useth entreaties: but the rich answereth roughly.
24 Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.
He that maketh many friends [doeth it] to his own destruction: but there is a friend that sticketh closer than a brother.

< Miyambo 18 >