< Miyambo 18 >

1 Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
Svémyslný hledá toho, což se jemu líbí, a ve všelijakou věc plete se.
2 Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
Nezalibuje sobě blázen v rozumnosti, ale v tom, což zjevuje srdce jeho.
3 Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
Když přijde bezbožný, přichází také pohrdání, a s lehkomyslným útržka.
4 Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
Slova úst muže vody hluboké, potok rozvodnilý pramen moudrosti.
5 Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
Přijímati osobu bezbožného není dobré, abys převrátil spravedlivého v soudu.
6 Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
Rtové blázna směřují k svadě, a ústa jeho bití se domluví.
7 Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
Ústa blázna k setření jemu, a rtové jeho osídlem duši jeho.
8 Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
Slova utrhače jsou jako ubitých, ale však sstupují do vnitřností života.
9 Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
Také ten, kdož jest nedbalý v práci své, bratr jest mrhače.
10 Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
Věže pevná jest jméno Hospodinovo; k němu se uteče spravedlivý, a bude povýšen.
11 Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
Zboží bohatého jest město pevné jeho, a jako zed vysoká v mysli jeho.
12 Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
Před setřením vyvyšuje se srdce člověka, ale před povýšením bývá ponížení.
13 Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
Kdož odpovídá něco, prvé než vyslyší, počítá se to za bláznovství jemu a za lehkost.
14 Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
Duch muže snáší nemoc svou, ducha pak zkormouceného kdo snese?
15 Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
Srdce rozumného dosahuje umění, a ucho moudrých hledá umění.
16 Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
Dar člověka uprostranňuje jemu, a před oblíčej mocných přivodí jej.
17 Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
Spravedlivý zdá se ten, kdož jest první v své při, ale když přichází bližní jeho, tedy stihá jej.
18 Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
Los pokojí svady, a mezi silnými rozeznává.
19 Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
Bratr křivdou uražený tvrdší jest než město nedobyté, a svárové jsou jako závora u hradu.
20 Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
Ovocem úst jednoho každého nasyceno bývá břicho jeho, úrodou rtů svých nasycen bude.
21 Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
Smrt i život jest v moci jazyka, a ten, kdož jej miluje, bude jísti ovoce jeho.
22 Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
Kdo nalezl manželku, nalezl věc dobrou, a navážil lásky od Hospodina.
23 Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
Poníženě mluví chudý, ale bohatý odpovídá tvrdě.
24 Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.
Ten, kdož má přátely, má se míti přátelsky, poněvadž přítel bývá vlastnější než bratr.

< Miyambo 18 >